< Masalimo 23 >
1 Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
A psalm for David. The Lord ruleth me: and I shall want nothing.
2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
He hath set me in a place of pasture. He hath brought me up, on the water of refreshment:
3 amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
He hath converted my soul. He hath led me on the paths of justice, for his own name’s sake.
4 Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
For though I should walk in the midst of the shadow of death, I will fear no evils, for thou art with me. Thy rod and thy staff, they have comforted me.
5 Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
Thou hast prepared a table before me against them that afflict me. Thou hast anointed my head with oil; and my chalice which inebriateth me, how goodly is it!
6 Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.
And thy mercy will follow me all the days of my life. And that I may dwell in the house of the Lord unto length of days.