< Masalimo 23 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
Psalam. Davidov. Jahve je pastir moj: ni u čem ja ne oskudijevam;
2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
na poljanama zelenim on mi daje odmora. Na vrutke me tihane vodi
3 amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
i krijepi dušu moju. Stazama pravim on me upravlja radi imena svojega.
4 Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
Pa da mi je i dolinom smrti proći, zla se ne bojim, jer si ti sa mnom. Tvoj štap i palica tvoja utjeha su meni.
5 Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
Trpezu preda mnom prostireš na oči dušmanima mojim. Uljem mi glavu mažeš, čaša se moja prelijeva.
6 Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.
Dobrota i milost pratit će mene sve dane života moga. U Jahvinu ću domu prebivati kroz dane mnoge.

< Masalimo 23 >