< Masalimo 22 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Wɔde ma dwonkyerɛfo. Wɔto no sɛnea wɔto “Adekyee forote” dwom. Dawid dwom. Me Nyankopɔn, me Nyankopɔn, adɛn nti na woagyaw me? Adɛn nti na me nkwagye ne wo ntam aware, adɛn na mʼapinisi nsɛm ne wo ntam aware?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
Me Nyankopɔn, misu frɛ wo awia, nanso wunnye me so, mefrɛ wo anadwo, nanso minnya ɔhome.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
Nanso wɔasi wo hene sɛ Ɔkronkronni; wo na Israel kamfo wo.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
Wo mu na yɛn agyanom de wɔn werɛ hyɛe; wogyee wo dii, na wugyee wɔn.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
Wosu frɛɛ wo na wugyee wɔn, wɔde wɔn ho too wo so na woanni wɔn nhuammɔ.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
Nanso meyɛ osunson, na menyɛ onipa nnipa bɔ me ahohora na wobu me animtiaa.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
Obiara a ohu me di me ho fɛw; wotwa me adapaa, wosow wɔn ti ka se:
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
“Ɔde ne ho to Awurade so; ma Awurade mmegye no. Ma ɔmmɛboa no, efisɛ ɔwɔ no mu anigye.”
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Wo na wuyii me fii awotwaa mu bae na womaa me de me ho too wo so bere a mitua me na nufu ano mpo.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
Efi mʼawo mu na wɔde me too wo so; efi me na yafunu mu, woayɛ me Nyankopɔn.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Ntwe wo ho mfi me ho! Efisɛ amane abɛn na ɔboafo nni baabi.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Anantwinini bebree atwa me ho ahyia; Basan anantwinini a wɔn ho yɛ den atwa me ho ahyia.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
Gyata a wɔbobɔ mu na wɔtetew wɔn hanam mu abuebue wɔn anom tɛtrɛɛ de kyerɛ me.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Wɔahwie me agu sɛ nsu, na me nnompe nyinaa ahodwow. Me koma adan amane; anan wɔ me mu.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Mʼanom ayow te sɛ kyɛmfɛre mu. Na me tɛkrɛma atare mʼanom. Wode me to owu mfutuma mu.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
Akraman atwa me ho ahyia, nnebɔneyɛfo kuw atwa me ahyia, wɔahwirew me nsa ne mʼanan mu.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
Me nnompe nyinaa gu petee mu; Mʼatamfo hwɛ me haa na wɔserew me.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
Wɔkyɛ me atade mu fa, na wɔbɔ me ntama so ntonto.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
Na wo, Awurade, ntwe wo ho; wone mʼahoɔden, bra ntɛm bɛboa me.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Gye me kra fi afoa ano; gye me nkwa a ɛsom bo no fi akraman tumi ase.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Gye me nkwa fi gyata anom; gye me fi ɛko mmɛn so.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
Mɛbɔ wo din akyerɛ me nuanom; mɛkamfo wo wɔ wɔn a wɔahyia hɔ no nyinaa anim.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Monkamfo Awurade, mo a musuro no no! Mo a moyɛ Yakob asefo, monhyɛ no anuonyam! Mo Israel asefo nyinaa, munni no ni!
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Ommuu nʼani nguu ɔmanehunufo ateetee so ɛ, ɔmfaa nʼanim nhintaw no; na mmom watie ne sufrɛ a ɔde rehwehwɛ mmoa no.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
Me botae a mede yi wo ayɛ wɔ bagua mu no fi wo; medi me bɔhyɛ so wɔ wɔn a wosuro wo no anim.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
Ahiafo bedidi na wɔamee; wɔn a wɔhwehwɛ Awurade beyi no ayɛ, mo koma nnya nkwa daa.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Asase ano nyinaa bɛkae akɔ Awurade nkyɛn, na amanaman no mmusua nyinaa bɛkotow nʼanim,
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
efisɛ tumi wɔ Awurade na odi amanaman so hene.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
Asase so adefo nyinaa bedidi na wɔasɔre no; wɔn a wɔkɔ dɔte mu nyinaa bebu nkotodwe nʼanim, wɔn a wɔrentumi mma nkwa mu.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Nkyirimma nyinaa bɛsom no; wɔbɛka Awurade ho asɛm akyerɛ awo ntoatoaso a edidi so.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
Wɔbɛka ne trenee akyerɛ nnipa a wonnya nwoo wɔn efisɛ ɔno na wayɛ.

< Masalimo 22 >