< Masalimo 22 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Pour le chef musicien; réglé sur « The Dœ of the Morning ». Un psaume de David. Mon Dieu, mon Dieu, pourquoi m'as-tu abandonné? Pourquoi es-tu si loin de me secourir, et des paroles de mes gémissements?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
Mon Dieu, je crie pendant le jour, mais tu ne réponds pas; dans la saison de la nuit, et je ne suis pas silencieux.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
Mais toi, tu es saint, vous qui habitez les louanges d'Israël.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
Nos pères avaient confiance en toi. Ils ont fait confiance, et vous les avez délivrés.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
Ils ont crié vers toi, et ils ont été délivrés. Ils ont eu confiance en vous, et n'ont pas été déçus.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
Mais moi, je suis un ver, et je ne suis pas un homme; un opprobre des hommes, et méprisé par le peuple.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
Tous ceux qui me voient se moquent de moi. Ils m'insultent de leurs lèvres. Ils secouent la tête en disant,
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
« Il se confie en Yahvé. Laissez-le le délivrer. Qu'il le sauve, puisqu'il se complaît en lui. »
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Mais c'est toi qui m'as fait sortir du ventre de ma mère. Tu m'as fait confiance alors que j'étais aux seins de ma mère.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
J'ai été jeté sur toi dès le sein de ma mère. Tu es mon Dieu depuis que ma mère m'a porté.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Ne t'éloigne pas de moi, car le malheur est proche. Car il n'y a personne pour aider.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
De nombreux taureaux m'ont entouré. De puissants taureaux de Bashan m'ont encerclé.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
Ils ouvrent largement la bouche contre moi, des lions déchirant leur proie et rugissant.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Je suis répandu comme de l'eau. Tous mes os sont déréglés. Mon cœur est comme de la cire. Il est fondu en moi.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Ma force est desséchée comme un pot de fleurs. Ma langue se colle au palais. Tu m'as amené dans la poussière de la mort.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
Car les chiens m'ont entouré. Une troupe de malfaiteurs m'a enfermé. Ils ont percé mes mains et mes pieds.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
Je peux compter tous mes os. Ils me regardent et me fixent.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
Ils partagent mes vêtements entre eux. Ils ont tiré au sort mes vêtements.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
Mais ne t'éloigne pas, Yahvé. Vous êtes mon aide. Dépêchez-vous de m'aider!
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Délivre mon âme de l'épée, ma précieuse vie du pouvoir du chien.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Sauve-moi de la gueule du lion! Oui, tu m'as sauvé des cornes des bœufs sauvages.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
Je proclamerai ton nom à mes frères. Au milieu de l'assemblée, je te louerai.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Vous qui craignez Yahvé, louez-le! Vous tous, descendants de Jacob, glorifiez-le! Restez en admiration devant lui, vous tous, descendants d'Israël!
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Car il n'a pas méprisé ni abhorré l'affliction des affligés, Il ne lui a pas non plus caché son visage; mais quand il a crié vers lui, il a entendu.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
Je te loue dans la grande assemblée. J'accomplirai mes vœux devant ceux qui le craignent.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
Les humbles mangeront et seront rassasiés. Ceux qui le cherchent loueront Yahvé. Que vos cœurs vivent à jamais.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Toutes les extrémités de la terre se souviendront et se tourneront vers Yahvé. Tous les parents des nations se prosterneront devant toi.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
Car le royaume appartient à Yahvé. Il est le chef des nations.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
Tous les riches de la terre mangeront et se prosterneront. Tous ceux qui descendent dans la poussière s'inclineront devant lui, même celui qui ne peut pas garder son âme en vie.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
La postérité le servira. On parlera du Seigneur aux générations futures.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
Ils viendront et annonceront sa justice à un peuple qui naîtra, car il l'a fait.