< Masalimo 22 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
To the choirmaster on [the] doe of the dawn a psalm of David. O God my God my why? have you forsaken me [are] far from deliverance my [the] words of cry of distress my.
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
O God my I call out by day and not you answer and night and not repose [belongs] to me.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
And you [are] holy sitting [the] praises of Israel.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
In you they trusted ancestors our they trusted and you delivered them.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
To you they cried out and they were delivered in you they trusted and not they were ashamed.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
And I [am] a worm and not a man a reproach of humankind and despised of a people.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
All [those who] see me they mock me they make a separation with a lip they shake a head.
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
Roll to Yahweh let him rescue him let him deliver him for he delights in him.
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
For you [were] drawing forth me from [the] belly [were] making trust me on [the] breasts of mother my.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
On you I was cast from [the] womb from [the] belly of mother my [have been] God my you.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
May not you be far from me for trouble [is] near for there not [is] a helper.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
They have surrounded me bulls many mighty [bulls] of Bashan they have encircled me.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
They have opened on me mouth their a lion tearing and roaring.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Like water I have been poured out and they have become dislocated all bones my it has become heart my like wax it has melted in [the] midst of inward parts my.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
It has dried up like earthenware - strength my and tongue my [has been] made to cling to jaws my and to [the] dust of death you put me.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
For they have surrounded me dogs a company of evil-doers they have encircled me (like a lion *L(D)*) hands my and feet my.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
I count all bones my they they look they look on me.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
They distribute clothes my to themselves and on clothing my they cast a lot.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
And you O Yahweh may not you be distant O strength my to help my make haste!
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Deliver! from [the] sword life my from [the] hand of a dog only [life] my.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Save me from [the] mouth of a lion and from [the] horns of wild oxen you have answered me.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
I will recount name your to brothers my in among [the] assembly I will praise you.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
O [those] fearing Yahweh - praise him O all [the] offspring of Jacob honor him and be afraid from him O all [the] offspring of Israel.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
For not he has despised and not he has detested [the] affliction of an afflicted [person] and not he has hidden face his from him and when cried for help he to him he heard.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
[is] from With you praise my in [the] assembly great vows my I will pay before [those] fearing him.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
They will eat humble [people] - so they may be satisfied they will praise Yahweh [those who] seek him may it live heart your for ever.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
They will remember - and they may turn to Yahweh all [the] ends of [the] earth so they may bow down before you all [the] clans of [the] nations.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
For [belongs] to Yahweh the kingship and [he is] ruling over the nations.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
They have eaten and they have bowed down - all [the] fat [people] of [the] earth before him they will bow down all [those who are] about to go down of dust and life his not he has preserved alive.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Offspring it will serve him it will be recounted of [the] Lord to the generation.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
They will come and they may declare righteousness his to a people about to be born that he has acted.