< Masalimo 22 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
[For the Chief Musician; set to "The Doe of the Morning." A Psalm by David.] My God, my God, why have you forsaken me? Why are you so far from helping me, and from the words of my groaning?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
My God, I cry in the daytime, but you do not answer; in the night season, and am not silent.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
But you are holy, you who inhabit the praises of Israel.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
Our fathers trusted in you. They trusted, and you delivered them.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
They cried to you, and escaped. They trusted in you, and were not put to shame.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
But I am a worm, and no man; scorned by people and despised by the people.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
All those who see me mock me. They insult me with their lips. They shake their heads, saying,
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
"He trusts in the LORD; let him deliver him. Let him rescue him, since he delights in him."
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
But you brought me out of the womb. You made me trust at my mother's breasts.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
I was thrown on you from my mother's womb. You are my God since my mother bore me.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Do not be far from me, for trouble is near. For there is none to help.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Many bulls have surrounded me. Mighty ones of Bashan have encircled me.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
They open their mouths wide against me, like a lion tearing prey and roaring.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
I am poured out like water, and all my bones are out of joint. My heart is like wax; it is melted within me.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
My strength is dried up like a potsherd, and my tongue sticks to the roof of my mouth; and you have brought me into the dust of death.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
For many dogs have surrounded me. A company of evildoers have enclosed me. They have pierced my hands and my feet.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
I can count all of my bones. They look and stare at me.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
They divide my clothes among themselves, and for my clothing they cast a lot.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
But do not be far off, LORD. You are my help: hurry to help me.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Deliver my soul from the sword, my precious life from the power of the dog.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Save me from the lion's mouth. Yes, from the horns of the wild oxen, you have answered me.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
I will declare your name to my brothers. In the midst of the assembly I will praise you.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
You who fear the LORD, praise him. All you descendants of Jacob, glorify him. Revere him, all you descendants of Israel.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
For he has not despised or detested the affliction of the afflicted, nor has he hidden his face from him; but when he cried to him, he heard.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
Of you comes my praise in the great assembly. I will pay my vows before those who fear him.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
The humble shall eat and be satisfied. They shall praise the LORD who seek after him. Let your hearts live forever.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Every part of the earth shall remember and turn to the LORD, and all the families of the nations shall worship before you.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
For the kingdom is the LORD's, and he is the ruler over the nations.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
All the prosperous of the earth shall eat and worship. All those who go down to the dust shall bow before him; and my soul shall live for him.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Posterity shall serve him. Future generations shall be told about the LORD.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
They shall come and shall declare his righteousness to a people that shall be born, for he has done it.

< Masalimo 22 >