< Masalimo 22 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
“To the chief musician upon Ayeleth-hashachar, a psalm of David.” My God, my God, why hast thou forsaken me? why art thou so far from saving me, and from the words of my loud complaint?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
O my God! I call in the day-time, but thou answerest not; and in the night I find no rest.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
But thou art holy, O thou that dwellest amidst the praises of Israel.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
In thee did our fathers trust: they trusted, and thou didst deliver them.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
Unto thee they cried, and were delivered: in thee they trusted, and were not put to shame.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
But I am a worm, and not a man, a reproach of men, and despised of people.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
All those who see me laugh me to scorn: they draw open their lips, they shake their head, [saying, ]
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
“Let him throw himself on the Lord, that he may deliver him: he will save him, for he delighteth in him.”
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Yea, thou art he that took me from the womb: thou hast been my trust when I hung on my mother's breasts.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
Upon thee was I cast from my birth: from my mother's womb art thou my God.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Oh be not far from me [now]; for distress is near; for there is none to help.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Many steers have encompassed me: the strong bulls of Bashan have beset me round.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
They have opened wide against me their mouth, [as] a ravenous and roaring lion.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Like water am I poured out, and all my bones are disjointed: my heart is become like wax, it is melted in the midst of my entrails.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Like a potsherd is my strength dried up; and my tongue cleaveth to my palate; and into the dust of death hast thou laid me down.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
For dogs have encompassed me; the assembly of the wicked have enclosed me: like lions [they threaten] my hands and my feet.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
I may number all my bones: [while] they stare and look upon me.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
They divide my clothes among themselves, and for my garment do they cast lots.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
But thou, O Lord, be not far from me: O [thou who art] my strength, hasten to my aid.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Deliver from the sword my life, from the power of the dog my solitary soul.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Save me from the lion's mouth; as thou hast answered me from the horns of the reem.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
I will relate thy name unto my brethren: in the midst of the congregation will I praise thee.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Ye that fear the Lord, praise him; all ye the seed of Jacob, glorify him; and be in dread of him, all ye the seed of Israel.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
For he hath not despised nor abhorred the affliction of the poor; neither hath he hidden his face from him; but when he cried unto him, he heard.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
Of thee shall be my praise in a great assembly: my vows will I pay in the presence of those who fear him.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
The meek shall eat and be satisfied; they who seek him shall praise the Lord: may your heart live for ever.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
All the ends of the world shall remember and return unto the Lord: and all the families of the nations shall bow themselves down before thee.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
For the kingdom is the Lord's, and he governeth the nations.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
All they that eat the fat of the earth shall bow themselves down; before him shall bend the knee all that are going down into the dust; for none can keep alive his own soul.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Distant ages shall serve him; there shall be related of the Lord unto future generations.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
They will come, and will tell his righteousness unto a people yet unborn, that he hath done this.