< Masalimo 22 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Unto the end, for the morning protection, a psalm for David. O God my God, look upon me: why hast thou forsaken me? Far from my salvation are the words of my sins.
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
O my God, I shall cry by day, and thou wilt not hear: and by night, and it shall not be reputed as folly in me.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
But thou dwellest in the holy place, the praise of Israel.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
In thee have our fathers hoped: they have hoped, and thou hast delivered them.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
They cried to thee, and they were saved: they trusted in thee, and were not confounded.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
But I am a worm, and no man: the reproach of men, and the outcast of the people.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
All they that saw me have laughed me to scorn: they have spoken with the lips, and wagged the head.
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
He hoped in the Lord, let him deliver him: let him save him, seeing he delighteth in him.
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
For thou art he that hast drawn me out of the womb: my hope from the breasts of my mother.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
I was cast upon thee from the womb. From my mother’s womb thou art my God,
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Depart not from me. For tribulation is very near: for there is none to help me.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Many calves have surrounded me: fat bulls have besieged me.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
They have opened their mouths against me, as a lion ravening and roaring.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
I am poured out like water; and all my bones are scattered. My heart is become like wax melting in the midst of my bowels.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
My strength is dried up like a potsherd, and my tongue hath cleaved to my jaws: and thou hast brought me down into the dust of death.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
For many dogs have encompassed me: the council of the malignant hath besieged me. They have dug my hands and feet.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
They have numbered all my bones. And they have looked and stared upon me.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
They parted my garments amongst them; and upon my vesture they cast lots.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
But thou, O Lord, remove not thy help to a distance from me; look towards my defence.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Deliver, O God, my soul from the sword: my only one from the hand of the dog.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Save me from the lion’s mouth; and my lowness from the horns of the unicorns.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
I will declare thy name to my brethren: in the midst of the church will I praise thee.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Ye that fear the Lord, praise him: all ye the seed of Jacob, glorify him.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Let all the seed of Israel fear him: because he hath not slighted nor despised the supplication of the poor man. Neither hath he turned away his face from me: and when I cried to him he heard me.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
With thee is my praise in a great church: I will pay my vows in the sight of them that fear him.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
The poor shall eat and shall be filled: and they shall praise the Lord that seek him: their hearts shall live for ever and ever.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
All the ends of the earth shall remember, and shall be converted to the Lord: And all the kindreds of the Gentiles shall adore in his sight.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
For the kingdom is the Lord’s; and he shall have dominion over the nations.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
All the fat ones of the earth have eaten and have adored: all they that go down to the earth shall fall before him.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
And to him my soul shall live: and my seed shall serve him.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
There shall be declared to the Lord a generation to come: and the heavens shall shew forth his justice to a people that shall be born, which the Lord hath made.