< Masalimo 22 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Přednímu zpěváku k času jitřnímu, žalm Davidův. Bože můj, Bože můj, pročež jsi mne opustil? Vzdálils se od spasení mého a od slov naříkání mého.
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
Bože můj, přes celý den volám, a neslyšíš, i v noci, a nemohu se utajiti.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
Ty zajisté jsi svatý, zůstávající vždycky k veliké chvále Izraelovi.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
V toběť doufali otcové naši, doufali, a vysvobozovals je.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
K tobě volávali, a spomáhals jim; v tobě doufali, a nebývali zahanbeni.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
Já pak červ jsem, a ne člověk, útržka lidská a povrhel vůbec.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
Všickni, kteříž mne vidí, posmívají se mi, ošklebují se, a hlavami potřásají, říkajíce:
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
Spustiltě se na Hospodina, nechť ho vysvobodí; nechať jej vytrhne, poněvadž se mu v něm zalíbilo.
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Ješto ty jsi, kterýž jsi mne vyvedl z života, ustaviv mne v doufání při prsích matky mé.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
Na tebeť jsem uvržen od narození svého, od života matky mé Bůh můj ty jsi.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Nevzdalujž se ode mne, nebo ssoužení blízké jest, a nemám spomocníka.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Obkličujíť mne býkové mnozí, silní volové z Bázan obstupují mne.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
Otvírají na mne ústa svá, jako lev rozsapávající a řvoucí.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Jako voda rozplynul jsem se, a rozstoupily se všecky kosti mé, a srdce mé jako vosk rozpustilo se u prostřed vnitřností mých.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Vyprahla jako střepina síla má, a jazyk můj přilnul k dásním mým, anobrž v prachu smrti položils mne.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
Nebo psi obskočili mne, rota zlostníků oblehla mne, zprobijeli ruce mé i nohy mé.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
Mohl bych sčísti všecky kosti své, oni pak hledí na mne, a dívají se mi.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
Dělí mezi sebou roucha má, a o můj oděv mecí los.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
Ale ty, Hospodine, nevzdalujž se, sílo má, přispěj k spomožení mému.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Vychvať od meče duši mou, a z moci psů jedinkou mou.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Zachovej mne od úst lva, a od rohů jednorožcových vyprosť mne.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
I budu vypravovati bratřím svým o jménu tvém, u prostřed shromáždění chváliti tě budu, řka:
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Kteříž se bojíte Hospodina, chvalte jej, všecko símě Jákobovo ctěte jej, a boj se ho všecka rodino Izraelova.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Nebo nepohrdá, ani se odvrací od trápení ztrápeného, aniž skrývá tváři své od něho, nýbrž když k němu volá, vyslýchá jej.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
O tobě chvála má v shromáždění velikém, sliby své plniti budu před těmi, kteříž se bojí tebe.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
Jísti budou tiší a nasyceni budou, chváliti budou Hospodina ti, kteříž ho hledají, živo bude srdce vaše na věky.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Rozpomenou a obrátí se k Hospodinu všecky končiny země, a skláněti se budou před ním všecky čeledi národů.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
Nebo Hospodinovo jest království, a onť panuje nad národy.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
Jísti budou a skláněti se před ním všickni tuční země, jemu se klaněti budou všickni sstupující do prachu, a kteříž duše své nemohou při životu zachovati.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Símě jejich sloužiti mu bude, a přičteno bude ku Pánu v každém věku.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
Přijdouť, a lidu, kterýž z nich vyjde, vypravovati budou spravedlnost jeho; nebo ji skutkem vykonal.

< Masalimo 22 >