< Masalimo 22 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
За първия певец по “Кошутата на зората”. Давидов псалом. Боже мой, Боже мой, защо си ме оставил? Защо стоиш далеч и не ми помагаш, Нито внимаваш на думите на охкането ми?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
Боже мой, викам денем, но не отговаряш, И нощем, но нямам отдих.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
Но Ти си Светият, Който си възцарен между Израилевите хваления.
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
На тебе уповаваха бащите ни Уповаваха, и Ти ги избави,
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
Към Тебе извикаха, и бяха избавени; На Тебе уповаваха, и не се посрамиха.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
А аз съм червей, а не човек, Укоряван от човеците, и презрян от людете.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
Всички, които ме гледат, ругаят ме, Отварят устните си, кимват с глава и казват:
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
Той упова на Господа: нека го избави; Нека го избави понеже има благоволение в него.
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Но Ти си, Който си ме извадил из утробата; Ти си ме научил да уповавам като бях на майчините си гърди,
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
На Тебе бях оставен от рождението си; От утробата на майка ми Ти си мой Бог.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Да се не отдалечиш от мене; защото скръбта е близо, Понеже няма помощник.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Много юнци ме обиколиха; Силни васански бикове ме окръжиха.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
Отвориха срещу мене устата си, Като лъв, който граби и реве.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Разлях се като вода, И разглобиха се всичките ми кости; Сърцето ми стана като восък, Разтопява се всред вътрешностите ми.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Силата ми изсъхна като черепка, И езикът ми прилепна за челюстите ми; И Ти си ме свел в пръстта на смъртта.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
Защото кучета ме обиколиха; Тълпа от злодейци ме окръжи; Прободоха ръцете ми и нозете ми.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
Мога да преброя всичките си кости, Хората се взират в мене и ме гледат.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
Разделиха си дрехите ми, И за облеклото ми хвърлиха жребие.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
Но Ти, Господи, да се не отдалечиш; Ти, сило моя, побързай да ми помогнеш.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Избави от меча душата ми, Живота ми от силата на кучето.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Избави ме от устата на лъва И от роговете не дивите волове. Ти си ме послушал!
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
Ще възвестявам името Ти на братята си; Всред събранието ще Те хваля.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Вие, които се боите от Господа, хвалете Го; Цяло Яковово потомство славете Го; И бойте Му се, всички вие от Израилевото потомство.
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Защото не е презрял и не се е отвърнал от скръбта на оскърбения, Нито е скрил лицето Си от него; Но послуша, когато извика той към Него.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
От Тебе е гдето принасям хваление в голямото събрание: Ще изпълня обреците си пред ония, които Му се боят.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
Смирените ще ядат и ще се наситят; Ще хвалят Господа ония, които Го търсят; Сърцето ви нека живее вечно.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Ще си спомнят и ще се обърнат към Господа Всичките земни краища, И ще се покланят пред Тебе Всичките племена на народите;
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
Защото царството е на Господа, И То владее над народите.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
Ще ядат и ще се поклонят всичките богати на земята; Пред Него ще се преклонят всички, които слизат в пръстта; А онзи, който не може да запази живота си,
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Неговото потомство ще Му слугува; Ще се приказва за Господа на идното поколение.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
Ще дойдат и ще известят правдата Му На люде, които ще се родят, казвайки, че Той е сторил това.