< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Que el Señor te oiga en el día de la angustia; que el nombre del Dios de Jacob te defienda;
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Que él te envíe ayuda desde el lugar santo, y te dé fuerzas desde Sión;
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Tenga en cuenta todas tus ofrendas y esté satisfecho con tu holocausto; (Selah)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Puede él darte el deseo de tu corazón y lleve a cabo todos tus propósitos.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
Nos alegraremos en tu salvación, y en el nombre de nuestro Dios levantaremos nuestras banderas: que el Señor te dé todas tus peticiones.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Ahora estoy seguro de que el Señor da la salvación a su rey; él le dará una respuesta desde su cielo santo con la fuerza de la salvación en su diestra.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Algunos ponen su fe en carruajes y algunos en caballos; mas nosotros confiaremos en el nombre del Señor nuestro Dios.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
Ellos flaquean y caen; mas nosotros nos levantamos, seguimos firmes y estamos en pie.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Ven a nuestra ayuda, Señor: que el Rey nos escuche cuando clamamos.

< Masalimo 20 >