< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Dem Musikmeister. Ein Psalm Davids. Jahwe erhöre dich am Tage der Not, es schütze dich der Name des Gottes Jakobs!
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Er sende dir Hilfe vom Heiligtum und vom Zion her stütze er dich.
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Er gedenke aller deiner Opfergaben und deine Brandopfer finde er fett. (Sela)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Er gebe dir, was dein Herz wünscht, und all' dein Vorhaben lasse er gelingen.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
Möchten wir jubeln dürfen über die Hilfe, die dir zu teil ward, und ob des Namens unseres Gottes die Banner schwingen. Jahwe erfülle alle deine Bitten!
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Nun weiß ich, daß Jahwe seinem Gesalbten hilft; er erhört ihn von seinem heiligen Himmel her durch Machtthaten, durch die Hilfe seiner Rechten.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Sie vertrauen auf Wagen und auf Rosse; wir aber rufen den Namen unseres Gottes an.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
Sie stürzten und fielen; wir aber richteten uns empor und blieben aufrecht.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Jahwe hilf dem König und erhöre uns, wenn wir rufen!

< Masalimo 20 >