< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
To victorie, the salm of Dauid. The Lord here thee in the dai of tribulacioun; the name of God of Jacob defende thee.
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Sende he helpe to thee fro the hooli place; and fro Syon defende he thee.
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Be he myndeful of al thi sacrifice; and thi brent sacrifice be maad fat.
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Yyue he to thee aftir thin herte; and conferme he al thi counsel.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
We schulen be glad in thin helthe; and we schulen be magnyfied in the name of oure God.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
The Lord fille alle thin axyngis; nowe Y haue knowe, that the Lord hath maad saaf his crist. He schal here hym fro his hooly heuene; the helthe of his riyt hond is in poweris.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Thes in charis, and these in horsis; but we schulen inwardli clepe in the name of oure Lord God.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
Thei ben boundun, and felden doun; but we han rise, and ben reisid.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Lord, make thou saaf the kyng; and here thou vs in the dai in which we inwardli clepen thee.

< Masalimo 20 >