< Masalimo 20 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
For the Chief Musician. A Psalm of David. The LORD answer thee in the day of trouble; the name of the God of Jacob set thee up on high;
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Send thee help from the sanctuary, and strengthen thee out of Zion;
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Remember all thy offerings, and accept thy burnt sacrifice; (Selah)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Grant thee thy heart’s desire, and fulfill all thy counsel.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
We will triumph in thy salvation, and in the name of our God we will set up our banners: the LORD fulfill all thy petitions.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Now know I that the LORD saveth his anointed; he wilt answer him from his holy heaven with the saving strength of his right hand.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Some [trust] in chariots, and some in horses: but we will make mention of the name of the LORD our God.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
They are bowed down and fallen: but we are risen, and stand upright.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Save, LORD: let the King answer us when we call.