< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
For the end, a Psalm of David. The Lord hear you in the day of trouble; the name of the God of Jacob defend you.
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Send you help from the sanctuary, and aid you out of Sion.
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Remember all your sacrifice, and enrich your whole burnt offering. (Pause)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Grant you according to your heart, and fulfill all your desire.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
We will exult in your salvation, and in the name of our God shall we be magnified: the Lord fulfil all your petitions.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Now I know that the Lord has saved his Christ: he shall hear him from his holy heaven: the salvation of his right hand is mighty.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Some [glory] in chariots, and some in horses: but we will glory in the name of the Lord our God.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
They are overthrown and fallen: but we are risen, and have been set upright.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
O Lord, save the king: and hear us in whatever day we call upon you.

< Masalimo 20 >