< Masalimo 20 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
For the choirmaster. A Psalm of David. May the LORD answer you in the day of trouble; may the name of the God of Jacob protect you.
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
May He send you help from the sanctuary and sustain you from Zion.
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
May He remember all your gifts and look favorably on your burnt offerings.
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
May He give you the desires of your heart and make all your plans succeed.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
May we shout for joy at your victory and raise a banner in the name of our God. May the LORD grant all your petitions.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Now I know that the LORD saves His anointed; He answers him from His holy heaven with the saving power of His right hand.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Some trust in chariots and others in horses, but we trust in the name of the LORD our God.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
They collapse and fall, but we rise up and stand firm.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
O LORD, save the king. Answer us on the day we call.