< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
【求賜君王勝利】 達味詩歌,交與樂官。 願上主在憂患之日,俯允你,願雅各伯的天主,保祐你!
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
願祂從聖所救護你,願祂由熙雍扶助你!
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
願祂追念你的一切祭獻,願祂悅納你的全燔祭獻!
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
願祂滿全你心中的志願,願祂玉成你的一切籌算!
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
我們要因你的勝利歡舞,奉我們天主的名豎立旗鼓:我的一切請求,願上主成就!
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
我深信上主必賞祂的受傅者獲勝,以無敵右手救拯,從神聖的高天俯聽。
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
他們或仗恃戰車,他們或仗恃戢馬;我們只以上主,我們天主的名自誇。
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
他們必將倒地喪命。我們卻將挺身立定。
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
上主,求你賜給君王獲勝,我們求您時,請您俯允我們。

< Masalimo 20 >