< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Чого то племе́на бунтують, а наро́ди задумують ма́рне?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Зе́мні царі повстають, і князі нара́джуються ра́зом на Господа та на Його Помаза́нця:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
„Позриваймо ми їхні кайда́ни, і поскидаймо із себе їхні пу́та!
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Але Той, Хто на небеса́х пробува́є — посміється, Владика їх висміє!
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Він тоді в Своїм гніві промовить до них, і настра́шить їх Він у Своїм пересе́рді:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
„Я ж помазав Свого Царя на Сіон, святу го́ру Свою.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Я хочу звістити постанову: Промовив до Мене Господь: Ти Мій Син, Я сьогодні Тебе породив.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Жадай Ти від Мене, — і дам Я наро́ди Тобі, як спадщину Твою, володі́ння ж Твоє — аж по кі́нці землі!
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Ти їх повбиваєш залізним жезло́м, потовчеш їх, як по́суд ганча́рський“.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
А тепер — помудрійте, царі, навчіться ви, су́дді землі:
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Служіть Господе́ві зо стра́хом, і радійте з тремті́нням!
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Шануйте Сина, щоб Він не розгнівався, і щоб вам не загинути в дорозі, бо гнів Його незаба́ром запа́литься. Блаженні усі, хто на Нього наді́ється!

< Masalimo 2 >