< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Varför larma hedningarna och tänka folken fåfänglighet?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Jordens konungar resa sig upp, och furstarna rådslå med varandra, mot HERREN och hans smorde:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
"Låt oss slita sönder deras bojor och kasta deras band ifrån oss."
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Han som bor i himmelen ler, HERREN bespottar dem.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Då talar han till dem i sin vrede, och i sin förgrymmelse förskräcker han dem:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
"Jag själv har insatt min konung på Sion, mitt heliga berg."
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Jag vill förtälja om vad beslutet är; HERREN sade till mig: "Du är min son, jag har i dag fött dig.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Begär av mig, så skall jag giva dig hedningarna till arvedel och jordens ändar till egendom.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Du skall sönderslå dem med järnspira, såsom lerkärl skall du krossa dem."
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Så kommen nu till förstånd, I konungar; låten varna eder, I domare på jorden.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Tjänen HERREN med fruktan, och fröjden eder med bävan.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Hyllen sonen, så att han icke vredgas och I förgåns på eder väg; ty snart kunde hans vrede upptändas. Saliga äro alla de som taga sin tillflykt till honom.

< Masalimo 2 >