< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Por que as nações se rebelam, e os povos planejam em vão?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Os reis da terra se levantam, e os governantes tomam conselhos reunidos contra o SENHOR, e contra seu Ungido, [dizendo]:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Rompamos as correntes deles, e lancemos fora de nós as cordas deles.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Aquele que está sentado nos céus rirá; o Senhor zombará deles.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Então ele lhes falará em sua ira; em seu furor ele os assombrará, [dizendo]:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
E eu ungi a meu Rei sobre Sião, o monte de minha santidade.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
E eu declararei o decreto do SENHOR: Ele me disse: Tu és meu Filho; eu hoje te gerei.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Pede-me, e eu te darei as nações [por] herança, e [por] tua propriedade os confins da terra.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Com cetro de ferro tu as quebrarás; como vaso de oleiro tu as despedaçarás;
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Portanto agora, reis, sede prudentes; vós, juízes da terra, deixai serdes instruídos.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Servi ao SENHOR com temor; e alegrai-vos com tremor.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Beijai ao Filho, para que ele não se ire, e pereçais [no] caminho; porque em breve a ira dele se acenderá. Bem-aventurados [são] todos os que nele confiam.

< Masalimo 2 >