< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Porque se amotinam as gentes, e os povos imaginam a vaidade?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Os reis da terra se levantam, e os príncipes consultam juntamente contra o Senhor e contra o seu ungido, dizendo:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Rompamos as suas ataduras, e sacudamos de nós as suas cordas.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Aquele que habita nos céus se rirá: o Senhor zombará deles.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Então lhes falará na sua ira, e no seu furor os turbará.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Eu porém ungi o meu Rei sobre o meu santo monte de Sião.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Recitarei o decreto: o Senhor me disse: Tu és meu Filho, eu hoje te gerei.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Pede-me, e eu te darei as nações por herança, e os fins da terra por tua possessão.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Tu os esmigalharás com uma vara de ferro; tu os despedaçarás como a um vaso de oleiro.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Agora pois, ó reis, sede prudentes; deixai-vos instruir, juízes da terra.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Servi ao Senhor com temor, e alegrai-vos com tremor.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Beijai ao Filho, para que se não ire, e pereçais no caminho, quando em breve se acender a sua ira: bem-aventurados todos aqueles que nele confiam.

< Masalimo 2 >