< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Perché tumultuano le nazioni, e meditano i popoli cose vane?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
I re della terra si ritrovano e i principi si consigliano assieme contro l’Eterno e contro il suo Unto, dicendo:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Rompiamo i loro legami e gettiamo via da noi le loro funi.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Colui che siede ne’ cieli ne riderà; il Signore si befferà di loro.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Allora parlerà loro nella sua ira, e nel suo furore li renderà smarriti:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Eppure, dirà, io ho stabilito il mio re sopra Sion, monte della mia santità.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Io spiegherò il decreto: L’Eterno mi disse: Tu sei il mio figliuolo, oggi io t’ho generato.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Chiedimi, io ti darò le nazioni per tua eredità e le estremità della terra per tuo possesso.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Tu le fiaccherai con uno scettro di ferro; tu le spezzerai come un vaso di vasellaio.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Ora dunque, o re, siate savi; lasciatevi correggere, o giudici della terra.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Servite l’Eterno con timore, e gioite con tremore.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Rendete omaggio al figlio, che talora l’Eterno non si adiri e voi non periate nella vostra via, perché d’un tratto l’ira sua può divampare. Beati tutti quelli che confidano in lui!

< Masalimo 2 >