< Masalimo 2 >
1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Pourquoi ce tumulte parmi les nations? Et pourquoi les peuples projettent-ils des choses vaines?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Les rois de la terre se sont levés, et les princes se sont concertés ensemble contre l'Éternel et contre son Oint.
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Rompons leurs liens, disent-ils, et jetons loin de nous leurs cordes!
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Celui qui est assis dans les cieux s'en rira; le Seigneur se moquera d'eux.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Alors il leur parlera dans sa colère; il les épouvantera dans son courroux.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Et moi, dira-t-il, j'ai sacré mon roi, sur Sion, ma montagne sainte.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Je publierai le décret de l'Éternel; il m'a dit: Tu es mon fils; aujourd'hui je t'ai engendré.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Demande-moi, et je te donnerai les nations pour héritage, et pour possession les bouts de la terre.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Tu les briseras avec un sceptre de fer, tu les mettras en pièces comme un vase de potier.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Maintenant donc, ô rois, ayez de l'intelligence; recevez instruction, juges de la terre.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Servez l'Éternel avec crainte, et réjouissez-vous avec tremblement.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Rendez hommage au Fils, de peur qu'il ne s'irrite, et que vous ne périssiez dans votre voie, quand sa colère s'enflammera tout à coup. Heureux tous ceux qui se confient en lui!