< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Pourquoi les nations s’agitent-elles en tumulte et les peuples méditent-ils de vains projets?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Les rois de la terre se soulèvent, et les princes tiennent conseil ensemble, contre Yahweh et contre son Oint.
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
« Brisons leurs liens, disent-ils, et jetons loin de nous leurs chaînes! »
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Celui qui est assis dans les cieux sourit, le Seigneur se moque d’eux.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Alors il leur parlera dans sa colère, et dans sa fureur il les épouvantera:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
« Et moi, j’ai établi mon roi, sur Sion, ma montagne sainte. »
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
« Je publierai le décret: Yahweh m’a dit: Tu es mon Fils, je t’ai engendré aujourd’hui.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Demande, et je te donnerai les nations pour héritage, pour domaine les extrémités de la terre.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Tu les briseras avec un sceptre de fer, tu les mettras en pièces comme le vase du potier. »
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Et maintenant, rois, devenez sages; recevez l’avertissement, juges de la terre.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Servez Yahweh avec crainte, tressaillez de joie avec tremblement.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Baisez le Fils, de peur qu’il ne s’irrite et que vous ne périssiez dans votre voie; Car bientôt s’allumerait sa colère; heureux tous ceux qui mettent en lui leur confiance.

< Masalimo 2 >