< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Miksi pakanat pauhaavat ja kansat turhia ajattelevat?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Maan kuninkaat nousevat, ruhtinaat yhdessä neuvottelevat Herraa ja hänen voideltuansa vastaan:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
"Katkaiskaamme heidän kahleensa, heittäkäämme päältämme heidän köytensä".
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Hän, joka taivaassa asuu, nauraa; Herra pilkkaa heitä.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Kerran hän on puhuva heille vihassansa, peljättävä heitä hirmuisuudessaan:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
"Minä olen asettanut kuninkaani Siioniin, pyhälle vuorelleni".
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Minä ilmoitan, mitä Herra on säätänyt. Hän lausui minulle: "Sinä olet minun poikani, tänä päivänä minä sinut synnytin.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Ano minulta, niin minä annan pakanakansat sinun perinnöksesi ja maan ääret sinun omiksesi.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Rautaisella valtikalla sinä heidät muserrat, niinkuin saviastian sinä särjet heidät."
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Tulkaa siis järkiinne, kuninkaat, maan tuomarit, ottakaa nuhteesta vaari.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Palvelkaa Herraa pelvolla ja iloitkaa vavistuksella.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Antakaa suuta pojalle, ettei hän vihastuisi ettekä te hukkuisi tiellänne. Sillä hänen vihansa syttyy äkisti. Autuaat ovat kaikki, jotka häneen turvaavat.

< Masalimo 2 >