< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Why do the heathen rage, and the people imagine a vain thing?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
The kings of the earth set themselves, and the rulers take counsel together, against the LORD, and against his anointed, saying,
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Let us break their bands asunder, and cast away their cords from us.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
He that sitteth in the heavens shall laugh: the Lord shall have them in derision.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Then shall he speak to them in his wrath, and trouble them in his great displeasure.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Yet have I set my king upon my holy hill of Zion.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
I will declare the decree: the LORD hath said to me, Thou art my Son; this day have I begotten thee.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Ask of me, and I shall give thee the heathen for thy inheritance, and the uttermost parts of the earth for thy possession.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Thou shalt break them with a rod of iron; thou shalt dash them in pieces like a potter’s vessel.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Be wise now therefore, O ye kings: be instructed, ye judges of the earth.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Serve the LORD with fear, and rejoice with trembling.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Kiss the Son, lest he be angry, and ye perish from the way, when his wrath is kindled but a little. Blessed are all they that put their trust in him.

< Masalimo 2 >