< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Why this turmoil of nations, this futile plotting of peoples,
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
with kings of the earth conspiring, and rulers consulting together, against the Lord and against his anointed,
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
to snap their bonds and fling their cords away?
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
He whose throne is in heaven laughs, the Lord mocks them.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Then he speaks to them in his wrath, and in his hot anger confounds them.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
“This my king is installed by me, on Zion my holy mountain.”
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
I will tell of the Lord’s decree. He said to me: “You are my son, this day I became your father.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Only ask, and I make you the heir of the nations, and lord of the world to its utmost bounds.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
You will break them with sceptre of iron, shatter them like pottery.”
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
So now, you kings, be wise: be warned, you rulers of earth.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Serve the Lord in awe, kiss his feet with trembling,
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
lest, angry, he hurl you to ruin; for soon will his fury blaze. Happy all who take refuge in him.

< Masalimo 2 >