< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Why do the nations rage, and the peoples plot in vain?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
The kings of the earth take a stand, and the rulers take counsel together, against the LORD, and against his Anointed:
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
"Let's tear off their shackles, and throw off their ropes from us."
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
The one who sits in the heavens laughs. The LORD scoffs at them.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Then he will speak to them in his anger, and terrify them in his wrath:
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
"But I myself have installed my king on Zion, my holy mountain."
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
I will tell of the decree. The LORD said to me, "You are my son. Today I have become your father.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Ask of me, and I will give the nations as your inheritance, and the farthest parts of the earth for your possession.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
You shall rule them with an iron scepter. You shall dash them in pieces like a potter's vessel."
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Now therefore, you kings, be wise; receive correction, you judges of the earth.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Serve the LORD with fear, and rejoice with trembling.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Do homage in purity, lest he be angry, and you perish in the way, when his anger is suddenly kindled. Blessed are all those who take refuge in him.

< Masalimo 2 >