< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Wherefore did the heathen rage, and the nations imagine vain things?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
The kings of the earth stood up, and the rulers gathered themselves together, against the Lord, and against his Christ;
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
[saying], Let us break through their bonds, and cast away their yoke from us.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
He that dwells in the heavens shall laugh them to scorn, and the Lord shall mock them.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Then shall he speak to them in his anger, and trouble them in his fury.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
But I have been made king by him on Sion his holy mountain,
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
declaring the ordinance of the Lord: the Lord said to me, Thou art my Son, to-day have I begotten thee.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Ask of me, and I will give thee the heathen [for] thine inheritance, and the ends of the earth [for] thy possession.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Thou shalt rule them with a rod of iron; thou shalt dash them in pieces as a potter's vessel.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Now therefore understand, ye kings: be instructed, all ye that judge the earth.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Serve the Lord with fear, and rejoice in him with trembling.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Accept correction, lest at any time the Lord be angry, and ye should perish from the righteous way: whensoever his wrath shall be suddenly kindled, blessed are all they that trust in him.

< Masalimo 2 >