< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Ba ham lae namtom rhoek khopo uh tih a poeyoek la namtu te a taeng uh?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Diklai manghai rhoek boeica rhoek loh thikat la tingtun uh, BOEIPA neh BOEIPAamah kah Messiah te a pai thil uh tih,
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
“Amih kah kuelrhui te bawt uh sih lamtah, mamih pum kah rhuivaeh voeih pa sih,” a ti uh.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Vaan ah aka ngol Boeipa loh amih te a nueih thil tih, a tamdaeng,
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Te vaengah A thintoek neh amih te a voek tih a thinsa neh amih te a let sak.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Te dongah kai loh kamah kah manghai te kamah kah Zion tlang cim ah ka hol coeng,” a ti.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
BOEIPA loh kai taengah, “Nang tah kamah ca ni, Tihnin ah kai loh nang kan sak,” a ti oltlueh te ka doek ni.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Kai taengah ham bih lamtah namtom boeih te na rho la kam paek vetih na khohut loh kho bawt kho le a pha ni.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Amih te thi caitueng neh na talh vetih, amsai kah hnopai bangla amih te na phop ni.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Te dongah manghai rhoek lungming la om uh saeh. Diklai laitloek rhoek toel uh laeh.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
BOEIPA te hinyahnah neh, omngaih neh, thuennah neh thothueng uh.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
A capa te mok pah, a thintoek ve, Mikpalap kah a thintoek loh n'dom vetih longpueng ah na milh ve. Anih dongah aka kuep boeih tah a yoethen.

< Masalimo 2 >