< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
למנצח מזמור לדוד השמים מספרים כבוד אל ומעשה ידיו מגיד הרקיע׃
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
יום ליום יביע אמר ולילה ללילה יחוה דעת׃
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
אין אמר ואין דברים בלי נשמע קולם׃
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
בכל הארץ יצא קום ובקצה תבל מליהם לשמש שם אהל בהם׃
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
והוא כחתן יצא מחפתו ישיש כגבור לרוץ ארח׃
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
מקצה השמים מוצאו ותקופתו על קצותם ואין נסתר מחמתו׃
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
תורת יהוה תמימה משיבת נפש עדות יהוה נאמנה מחכימת פתי׃
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
פקודי יהוה ישרים משמחי לב מצות יהוה ברה מאירת עינים׃
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
יראת יהוה טהורה עומדת לעד משפטי יהוה אמת צדקו יחדו׃
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
הנחמדים מזהב ומפז רב ומתוקים מדבש ונפת צופים׃
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
גם עבדך נזהר בהם בשמרם עקב רב׃
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
שגיאות מי יבין מנסתרות נקני׃
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
גם מזדים חשך עבדך אל ימשלו בי אז איתם ונקיתי מפשע רב׃
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
יהיו לרצון אמרי פי והגיון לבי לפניך יהוה צורי וגאלי׃

< Masalimo 19 >