< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
למנצח מזמור לדוד ב השמים מספרים כבוד-אל ומעשה ידיו מגיד הרקיע
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
יום ליום יביע אמר ולילה ללילה יחוה-דעת
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
אין-אמר ואין דברים בלי נשמע קולם
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
בכל-הארץ יצא קום ובקצה תבל מליהם לשמש שם-אהל בהם
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
והוא--כחתן יצא מחפתו ישיש כגבור לרוץ ארח
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
מקצה השמים מוצאו--ותקופתו על-קצותם ואין נסתר מחמתו
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
תורת יהוה תמימה משיבת נפש עדות יהוה נאמנה מחכימת פתי
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
פקודי יהוה ישרים משמחי-לב מצות יהוה ברה מאירת עינים
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
יראת יהוה טהורה--עומדת לעד משפטי-יהוה אמת צדקו יחדו
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
הנחמדים--מזהב ומפז רב ומתוקים מדבש ונפת צופים
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
גם-עבדך נזהר בהם בשמרם עקב רב
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
שגיאות מי-יבין מנסתרות נקני
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
גם מזדים חשך עבדך-- אל-ימשלו-בי אז איתם ונקיתי מפשע רב
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
יהיו לרצון אמרי-פי והגיון לבי לפניך יהוה צורי וגאלי

< Masalimo 19 >