< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
Les cieux racontent la gloire de Dieu, et l'étendue fait connaître l'œuvre de ses mains.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Le jour parle au jour, et la nuit enseigne la nuit.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
Ce n'est pas un langage, ce ne sont pas des paroles dont la voix ne s'entende pas.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Leur voix se répand par toute la terre, et leurs paroles jusqu'aux extrémités du monde. Là, il a dressé un pavillon pour le soleil.
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
Et lui, il est comme un époux sortant de sa chambre nuptiale; il se réjouit, comme un héros, de parcourir la carrière.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
Il part de l'un des bouts des cieux, et son tour s'achève à l'autre bout; et rien ne se dérobe à sa chaleur.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
La loi de l'Éternel est parfaite, elle restaure l'âme; le témoignage de l'Éternel est sûr, il donne de la sagesse aux simples.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
Les ordonnances de l'Éternel sont droites, elles réjouissent le cœur; le commandement de l'Éternel est pur, il éclaire les yeux.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
La crainte de l'Éternel est pure, elle subsiste à perpétuité; les jugements de l'Éternel ne sont que vérité, ils sont tous également justes.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
Ils sont plus désirables que l'or, et que beaucoup d'or fin; plus doux que le miel, que ce qui découle des rayons de miel.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
Aussi ton serviteur est éclairé par eux; il y a un grand salaire dans leur observation.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Qui connaît ses fautes commises par erreur? Pardonne-moi mes fautes cachées.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
Préserve aussi ton serviteur des péchés d'orgueil; qu'ils ne dominent point sur moi; alors je serai intègre et innocent de grands péchés.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
Que les paroles de ma bouche et la méditation de mon cœur te soient agréables, ô Éternel, mon rocher et mon rédempteur!

< Masalimo 19 >