< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
to/for to conduct melody to/for David [the] heaven to recount glory God and deed: work hand his to tell [the] expanse
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
day to/for day to bubble word and night to/for night to explain knowledge
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
nothing word and nothing word without to hear: hear voice their
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
in/on/with all [the] land: country/planet to come out: speak line their and in/on/with end world speech their to/for sun to set: make tent in/on/with them
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
and he/she/it like/as son-in-law to come out: come from canopy his to rejoice like/as mighty man to/for to run: run way
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
from end [the] heaven exit his and circuit his upon end their and nothing to hide from heat his
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
instruction LORD unblemished to return: rescue soul testimony LORD be faithful be wise simple
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
precept LORD upright to rejoice heart commandment LORD pure to light eye
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
fear LORD pure to stand: stand to/for perpetuity justice: judgement LORD truth: certain to justify together
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
[the] to desire from gold and from pure gold many and sweet from honey and honey honeycomb
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
also servant/slave your to warn in/on/with them in/on/with to keep: obey them consequence many
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
error who? to understand from to hide to clear me
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
also from arrogant to withhold servant/slave your not to rule in/on/with me then to finish and to clear from transgression many
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
to be to/for acceptance word lip my and meditation heart my to/for face your LORD rock my and to redeem: redeem my

< Masalimo 19 >