< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
For the Chief Musician. A Psalm of David. The heavens declare the glory of God; and the firmament sheweth his handywork.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Day unto day uttereth speech, and night unto night sheweth knowledge.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
There is no speech nor language; their voice cannot be heard.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Their line is gone out through all the earth, and their words to the end of the world. In them hath he set a tabernacle for the sun,
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
Which is as a bridegroom coming out of his chamber, and rejoiceth as a strong man to run his course.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
His going forth is from the end of the heaven, and his circuit unto the ends of it: and there is nothing hid from the heat thereof.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The law of the LORD is perfect, restoring the soul: the testimony of the LORD is sure, making wise the simple.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The precepts of the LORD are right, rejoicing the heart: the commandment of the LORD is pure, enlightening the eyes.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The fear of the LORD is clean, enduring for ever: the judgments of the LORD are true, [and] righteous altogether.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
More to be desired are they than gold, yea, than much fine gold: sweeter also than honey and the honeycomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
Moreover by them is thy servant warned: in keeping of them there is great reward.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who can discern [his] errors? clear thou me from hidden [faults].
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
Keep back thy servant also from presumptuous [sins]; let them not have dominion over me: then shall I be perfect, and I shall be clear from great transgression.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
Let the words of my mouth and the meditation of my heart be acceptable in thy sight, O LORD, my rock, and my redeemer.

< Masalimo 19 >