< Masalimo 19 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
“For the leader of the music. A psalm of David.” The heavens declare the glory of God; The firmament showeth forth the work of his hands.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Day uttereth instruction unto day, And night showeth knowledge unto night.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
They have no speech nor language, And their voice is not heard;
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Yet their sound goeth forth to all the earth, And their words to the ends of the world. In them hath he set a tabernacle for the sun,
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
Which cometh forth like a bridegroom from his chamber, And rejoiceth, like a strong man, to run his course.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
He goeth forth from the extremity of heaven, And maketh his circuit to the end of it; And nothing is hid from his heat.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The law of the LORD is perfect, reviving the soul; The precepts of the LORD are sure, making wise the simple;
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The statutes of the LORD are right, rejoicing the heart; The commandments of the LORD are pure, enlightening the eyes;
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The fear of the LORD is clean, enduring for ever; The judgments of the LORD are true and righteous altogether.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
More precious are they than gold; yea, than much fine gold; Sweeter than honey and the honeycomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
By them also is thy servant warned, And in keeping of them there is great reward.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who knoweth his own offences? Oh, cleanse thou me from secret faults!
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
Keep back also thy servant from presumptuous sins; Let them not have dominion over me! Then shall I be upright; I shall not be polluted with gross transgression.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
May the words of my mouth and the meditation of my heart Be acceptable in thy sight, O LORD, my strength and my redeemer!