< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
[For the Chief Musician. A Psalm by David.] The heavens declare the glory of God. The expanse shows his handiwork.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Day after day they pour forth speech, and night after night they display knowledge.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
There is no speech nor language, where their voice is not heard.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Their voice has gone out to all the earth, their words to the farthest part of the world. In them he has set a tent for the sun,
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
which is as a bridegroom coming out of his chamber, like a strong man rejoicing to run his course.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
His going forth is from the end of the heavens, his circuit to its ends; There is nothing hidden from its heat.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The LORD's Law is perfect, restoring the soul. The LORD's testimony is sure, making wise the simple.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The LORD's precepts are right, rejoicing the heart. The LORD's commandment is pure, enlightening the eyes.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The fear of the LORD is clean, enduring forever. The LORD's ordinances are true, and righteous altogether.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
More to be desired are they than gold, yes, than much fine gold; sweeter also than honey and the extract of the honeycomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
Moreover by them is your servant warned. In keeping them there is great reward.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who can discern his errors? Forgive me from hidden errors.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
Keep back your servant also from presumptuous sins. Let them not have dominion over me. Then I will be upright. I will be blameless and innocent of great transgression.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
Let the words of my mouth and the meditation of my heart be acceptable in your sight always, LORD, my rock and my redeemer.

< Masalimo 19 >