< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
Unto the end. A Psalm of David. The heavens describe the glory of God, and the firmament announces the work of his hands.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Day proclaims the word to day, and night to night imparts knowledge.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
There are no speeches or conversations, where their voices are not being heard.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Their sound has gone forth through all the earth, and their words to the ends of the world.
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
He has placed his tabernacle in the sun, and he is like a bridegroom coming out of his bedroom. He has exulted like a giant running along the way;
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
his departure is from the summit of heaven. And his course reaches all the way to its summit. Neither is there anyone who can hide himself from his heat.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The law of the Lord is immaculate, converting souls. The testimony of the Lord is faithful, providing wisdom to little ones.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The justice of the Lord is right, rejoicing hearts. The precepts of the Lord are brilliant, enlightening the eyes.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The fear of the Lord is holy, enduring for all generations. The judgments of the Lord are true, justified in themselves:
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
desirable beyond gold and many precious stones, and sweeter than honey and the honeycomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
For, indeed, your servant keeps them, and in keeping them, there are many rewards.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who can understand transgression? From my hidden faults, cleanse me, O Lord,
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
and from those of others, spare your servant. If they will have no dominion over me, then I will be immaculate, and I will be cleansed from the greatest transgression.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
And the eloquence of my mouth will be so as to please, along with the meditation of my heart, in your sight, forever, O Lord, my helper and my redeemer.

< Masalimo 19 >