< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
Ljubil te bom, oh Gospod, moja moč.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
Gospod je moja skala, moja trdnjava in moj osvoboditelj, moj Bog, moja moč, v katero bom zaupal, moj ščit in rog rešitve moje duše in moj visoki stolp.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Klical bom h Gospodu, ki je vreden, da je hvaljen. Tako bom rešen pred svojimi sovražniki.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Obdale so me bridkosti smrti in poplave brezbožnih ljudi so me prestrašile.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Obkrožile so me bridkosti pekla. Zanke smrti so me ovirale. (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
V svoji stiski sem klical h Gospodu in jokal k svojemu Bogu. Iz svojega templja je slišal moj glas in moj jok je prišel predenj, celó v njegova ušesa.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Potem se je zemlja stresla in zatrepetala, tudi temelji gora so se premaknili in bili streseni, ker je bil ogorčen.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Iz njegovih nosnic je izšel dim in ogenj iz njegovih ust je požiral. Ogorki so bili prižgani z njim.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Uklonil je tudi nebo in prišel dol. Tema je bila pod njegovimi stopali.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Jezdil je na kerubu in letel. Da, letel je na perutih vetra.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
Temo je naredil [za] svoj skriti kraj, njegov paviljon okoli njega so bile temne vode in gosti oblaki neba.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
Ob sijaju, ki je bil pred njim, so šli mimo njegovi gosti oblaki, zrna toče in ognjeno oglje.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Gospod je tudi zagrmel v nebesih in Najvišji je dal svoj glas, zrna toče in ognjeno oglje.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Da, poslal je svoje puščice in jih razkropil in izstrelil bliske ter jih porazil.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Potem so bila vidna rečna korita in temelji zemeljskega [kroga] so bili odkriti ob tvojem oštevanju, oh Gospod, ob pišu diha iz tvojih nosnic.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Poslal je od zgoraj, me vzel, me potegnil iz mnogih voda.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
Osvobodil me je pred mojim močnim sovražnikom in pred temi, ki so me sovražili, kajti zame so bili premočni.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Ovirali so me na dan moje katastrofe. Toda Gospod je bil moja opora.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Privedel me je tudi na velik kraj, osvobodil me je, ker se je razveseljeval v meni.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Gospod me je nagradil glede na mojo pravičnost, glede na čistost mojih rok mi je poplačal.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
Kajti obdržal sem Gospodove poti in se nisem zlobno oddvojil od svojega Boga.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
Kajti vse njegove sodbe so bile pred menoj in njegovih zakonov nisem odvrnil od sebe.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Pred njim sem bil tudi pošten in se varoval pred svojo krivičnostjo.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Zaradi tega mi je Gospod poplačal glede na mojo pravičnost, glede na čistost mojih rok v svojem pogledu.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Z usmiljenim se boš pokazal usmiljenega, s poštenim človekom se boš pokazal poštenega,
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
s čistim se boš pokazal čistega in s kljubovalnim se boš pokazal kljubovalnega.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
Kajti rešil boš stiskano ljudstvo, toda ponižal boš vzvišene poglede.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Kajti prižgal boš mojo svečo. Gospod, moj Bog, bo razsvetlil mojo temo.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Kajti s teboj sem tekel skozi krdelo in s svojim Bogom sem preskočil zid.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
Glede Boga, njegova pot je popolna. Gospodova beseda je preizkušena; on je ščit vsem, ki zaupajo vanj.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Kajti kdo je Bog, razen Gospoda? Ali kdo je skala, razen našega Boga?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Bog je ta, ki me opasuje z močjo in moje poti dela popolne.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Moja stopala dela podobna stopalom košute in me postavlja na moja visoka mesta.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Úči moje roke za vojno, tako da je jeklen lok zlomljen z mojimi lakti.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Dal si mi tudi ščit tvoje rešitve duše in tvoja desnica me podpira in tvoja blagost me je naredila velikega.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Pod menoj si razširil moje korake, da moja stopala niso zdrsnila.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
Zasledoval sem svoje sovražnike in jih dohitevam. Niti se nisem ponovno obrnil, dokler niso bili uničeni.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
Ranil sem jih, da niso mogli vstati. Padli so pod moja stopala.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
Kajti opasal si me z močjo za boj. Podjarmil si mi tiste, ki vstajajo zoper mene.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Prav tako si mi dal vratove mojih sovražnikov, da lahko uničim te, ki me sovražijo.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
Vpili so, toda nikogar ni bilo, da jih reši, celó h Gospodu, toda ni jim odgovoril.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Potem sem jih mlatil, majhne kakor prah pred vetrom. Spodil sem jih kakor nesnago na ulicah.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Osvobodil si me pred človeškimi prepiri in me naredil za poglavarja poganom. Ljudstvo, ki ga nisem poznal, mi bo služilo.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
Takoj, ko bodo zaslišali o meni, me bodo ubogali. Tujci se mi bodo podredili.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Tujci bodo bledeli in prestrašeni bodo iz svojih ograjenih prostorov.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
Gospod živi in blagoslovljena bodi moja skala in vzvišen naj bo Bog rešitve moje duše.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
To je Bog, ki me maščuje in ljudstva podjarmlja pod menoj.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Osvobaja me pred mojimi sovražniki. Da, dviguješ me nad tiste, ki se dvigujejo zoper mene. Osvobodil si me pred nasilnežem.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Zatorej se ti bom zahvaljeval med pogani, oh Gospod in prepeval hvalnice tvojemu imenu.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
Svojemu kralju on daje veliko osvoboditev in izkazuje usmiljenje svojemu maziljencu Davidu in njegovemu semenu na vékomaj.

< Masalimo 18 >