< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
Przedniejszemu śpiewakowi pieśń Dawida, sługi Pańskiego, który mówił do Pana słowa tej pieśni onego dnia, gdy go Pan wyrwał z rąk wszystkich nieprzyjaciół jego, i z ręki Saulowej; i rzekł: Rozmiłuję się ciebie, Panie, mocy moja!
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
Pan opoką moją, twierdzą moją, i wybawicielem moim; Bóg mój skała moja, w nim będę ufał; tarcza moja, i róg zbawienia mego, ucieczka moja.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Wzywałem Pana chwalebnego, a od nieprzyjaciół moich byłem wybawiony.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Ogarnęły mię były boleści śmierci, a potoki niepobożnych zatrwożyły mię.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Boleści grobu ogarnęły mię były, zachwyciły mię sidła śmierci. (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
W utrapieniu mojem wzywałem Pana, i wołałem do Boga mego; wysłuchał z kościoła swego głos mój, a wołanie moje przed oblicznością jego przyszło do uszów jego.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Tedy się ziemia wzruszyła i zadrżała, a fundamenty gór zatrząsnęły się, i wzruszyły się od gniewu jego.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Występował dym z nozdrzy jego, węgle się rozpaliły od niego.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Nakłonił niebios, i zstąpił, a ciemność była pod nogami jego.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
A wsiadłszy na Cheruba, latał; latał na skrzydłach wiatrowych.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
Uczynił sobie z ciemności ukrycie, około siebie namiot swój z ciemnych wód, i z gęstych obłoków.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
Od blasku przed nim rozeszły się obłoki jego, grad i węgle ogniste.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
I zagrzmiał na niebie Pan, a Najwyższy wydał głos swój, grad i węgle ogniste.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Wypuścił strzały swe, i rozproszył ich, a błyskawicami gęstemi rozgromił ich.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
I okazały się głębokości wód, a odkryte są grunty świata na fukanie twoje, Panie! i na tchnienie wiatru nozdrzy twoich.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Posławszy z wysokości zachwycił mię; wyciągnął mię z wód wielkich.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
Wyrwał mię od mocnego nieprzyjaciela mego, i od tych, którzy mię mieli w nienawiści, choć byli mocniejszymi nad mię.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Uprzedzili mię byli w dzień utrapienia mego; ale Pan był podporą moją.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Wywiódł mię na przestrzeństwo; wyrwał mię, iż mię umiłował.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Nagrodził mi Pan według sprawiedliwości mojej; według czystości rąk moich oddał mi.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
Bom strzegł dróg Pańskich, anim odstąpił niezbożnie od Boga mego.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
Bom miał wszystkie sądy jego przed oczyma memi, a ustaw jego nie odrzucałem od siebie.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Owszem, byłem szczerym przed nim, a strzegłem się od nieprawości mojej.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Przetoż oddał mi Pan według sprawiedliwości mojej, według czystości rąk moich, która była przed oczyma jego.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Ty, Panie! z miłosiernym miłosiernie się obejdziesz, a z mężem szczerym szczerze sobie postąpisz.
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Z uprzejmym uprzejmie się obejdziesz, a z przewrotnym przewrotnie sobie postąpisz;
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
Albowiem ty lud utrapiony wybawisz, a oczy wyniosłe poniżysz.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Ty zaiste rozświecisz pochodnię moję; Pan, Bóg mój, oświeci ciemności moje.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Gdyż z tobą przebiłem się przez wojsko, a z Bogiem moim przeskoczyłem mur.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
Droga Boża doskonała jest; słowo Pańskie jest ogniem wypławione. Tarczą jest wszystkich, którzy w nim ufają.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Bo któż jest Bóg, oprócz Pana? a kto opoką, oprócz Boga naszego?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
On jest Bogiem, który mię opasuje mocą, a czyni prostą drogę moję.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Krzepi nogi moje jako jelenie, a na wysokich miejscach moich stawia mię.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Çwiczy ręce moje do boju, tak, iż kruszę łuk miedziany ramionami swemi.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Dałeś mi też tarcz zbawienia twego, a prawica twoja podpierała mię, i dobrotliwość twoja uwielmożyła mię.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Rozszerzyłeś kroki moje podemną, tak, że się nie zachwiały golenie moje.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
Goniłem nieprzyjaciół moich, a doścignąłem ich: i nie wróciłem się, ażem ich wytracił.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
Poraziłem ich tak, iż nie mogli powstać; upadli pod nogi moje.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
Tyś mię opasał mocą ku bitwie; powstawających przeciwko mnie obaliłeś pod mię.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Podałeś mi tył nieprzyjaciół moich, abym tych, którzy mię nienawidzą, wykorzenił.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
Wołalić, ale nie był, ktoby ich wybawił; do Pana, ale ich nie wysłuchał.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
I potarłem ich, jako proch od wiatru; jako błoto na ulicach podeptałem ich.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Wyrwałeś mię od zwad ludzkich, a postawiłeś mię głową narodom; lud, któregom nie znał, służył mi.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
Skoro usłyszeli, byli mi posłuszni; cudzoziemcy obłudnie mi się poddawali.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Cudzoziemcy opadli, a drżeli w zamknieniach swoich.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
Żyje Pan, błogosławiona opoka moja; przetoż niech będzie wywyższony Bóg zbawienia mego.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
Bóg jest, który mi zleca pomsty, i podbija mi narody.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Tyś wybawiciel mój od nieprzyjaciół moich; tyś mię nad powstawających przeciwko mnie wywyższył; od męża drapieżnego wyrwałeś mię.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Przetoż cię, Panie! będę wyznawał między narodami, a będę śpiewał imieniowi twemu.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
Boś zacnie wybawił króla swego, a czynisz miłosierdzie pomazańcowi swemu Dawidowi, i nasieniu jego, aż na wieki.

< Masalimo 18 >