< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
Ay-ayatenka, O Yahweh, a pagtaudan iti pigsak.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
Ni Yahweh ti dakkel a batok, ti sarikedkedko, ti mangiyeg kaniak iti pannakasalaknib; isuna ti Diosko, ti dakkel a batok; Agkamangak kenkuana. Isuna ti kalasagko, ti sara ti pannakaisalakanko, ken ti natibker a pagkamangak.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Umawagak kenni Yahweh a maikari a mapadayawan, ket maisalakanakto manipud kadagiti kabusorko.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Pinulipulannak dagiti tali ni patay, ket linipusnak ti naapres a danum ti pannakadadael.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Naipulipul kaniak dagiti tali ti sheol; napalab-oganak iti silo ni patay. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
Iti pannakariribukko, immawagak kenni Yahweh; nagpatulongak iti Diosko. Nangngegna ti timekko manipud iti templona; nakadanon iti presensiana ti panagpatulongko; dimmanon daytoy kadagiti lapayagna.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Kalpasanna, nagun-gon ken nadayeg ti daga; nadayeg pay ken nagungon dagiti pundasion dagiti banbantay gapu ta nakaunget ti Dios.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Rimmuar ti asuk manipud iti agongna, ken gumilgil-ayab nga apuy ti rimuar iti ngiwatna. Dimmarang dagiti beggang gapu iti daytoy.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Linukatanna dagiti langit ket bimmaba, ken adda napuskol a sipnget iti sakaananna.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Nakasakay isuna iti maysa a kerubim ket timmayab; nagpangato isuna kadagiti payyak ti angin.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
Pinagbalinna ti sipnget nga abbongna, napuskol nga ulep a napno iti danum iti tangatang.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
Manipud iti kimat iti sangoananna, nagtinnag dagiti uraro ken beggang.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Naggurruod ni Yahweh kadagiti langlangit! Nagpukkaw ti Kangangatoan ket nangibaon kadagiti uraro ken kimat. Imbiatna dagiti panana ket nawara dagiti kabusorna;
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
adu a kimat ti nangwarawara kadakuada.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Kalpasanna, nagparang dagiti pagayusan ti danum; nawaknitan dagiti pundasion ti lubong iti pukkawmo a makigubat, Yahweh— iti napigsa nga anges dagiti agongmo.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Inggaw-atna manipud ngato; iniggamannak! Ginuyodnak manipud iti naapres a danum.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
Inispalnak manipud iti napigsa a kabusorko, manipud kadagiti gumurgura kaniak, ta napigsada unay para kaniak.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Immayda a maibusor kaniak iti aldaw ti pannakariribukko ngem ni Yahweh ti saranayko!
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Winayawayaannak iti nalawa a nawaya a lugar; insalakannak gapu ta naay-ayo isuna kaniak.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Ginun-gonaannak ni Yahweh gapu iti kinalintegko; pinabaronak gapu ta nadalus dagiti imak.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
Ta sinalimetmetak dagiti dalan ni Yahweh ken saanak a sidadangkes a timmallikud iti Diosko.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
Ta adda idin iti sangoanak dagiti nalinteg a bilinna; kasta met dagiti alagadenna, saanak a timmallikod kadagitoy.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Saanak met a nagkurang iti sangoananna, ken inyadayok ti bagik iti basol.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Ngarud, insublinak ni Yahweh gapu iti kinalintegko, gapu ta nadalus dagiti imak iti imatangna.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Iti siasinoman a napudno, iparangmo ti bagim a napudno; iti maysa a tao nga awan pakapilawanna, iparangmo ti bagim nga awan pakapilawanna.
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Iti siasinoman a nasin-aw, iparangmo ti bagim a nasin-aw; ngem nasikapka iti siasinoman a nakillo.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
Ta isalakanmo dagiti maparparigat a tattao, ngem ipababam dagiti addaan napannakkel a matmata!
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Ta gangtam ti pagsilawak; Lawagan ni Yahweh a Diosko ti kasipngetak.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Ta kabaelak a lasaten ti maysa a bangen babaen kenka; babaen iti Diosko kabaelak a lagtoen ti maysa a pader.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
Maipapan iti Dios: naan-anay ti wagasna. Nasin-aw ti sao ni Yahweh! Isuna ti kalasag iti amin a kumamang kenkuana.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Ta siasino ti Dios no di laeng ni Yahweh? Siasino ti maysa a dakkel a bato no di laeng ti Diostayo?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Isu ti Dios a mangmangted iti pigsak a kasla maysa a barikes, a mangikabkabil kadagiti awan pakapilawanna a tattao iti dalanna.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Papartakenna dagiti sakak a kasla maysa nga ugsa ken ikabilnak kadagiti banbantay!
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Sansanayenna dagiti imak para iti gubat ken dagiti takiagko a mangbiat iti pana a bronse.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Intedmo kaniak ti kalasag ti panangisalakanmo. Tinulongannak ti makannawan nga imam, ken pinatan-oknak ti pabormo.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Nangaramidka iti nalawa a lugar a pagbaddekak tapno saan a maikaglis dagiti sakak.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
Kinamatko dagiti kabusorko ken tiniliwko ida; Saanak a nagsanud agingga a nadadaelda.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
Rinumekko ida tapno saandan a makabangon; natuangda iti sakaanak.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
Ta inikkannak ti pigsak a kasla barikes a pakigubat; inkabilmo iti babaek dagiti tumakder a maibusor kaniak.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Intedmo kaniak dagiti teltel dagiti kabusorko; Pinarmekko dagiti gumurgura kaniak.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
Nagpaarayatda, ngem awan ti uray maysa a nangisalakan kadakuada; immawagda kenni Yahweh, ngem saanna ida a sinungbatan.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Rinumekko ida iti napino a kasla tapuk iti angin; Inbellengko ida a kasla pitak kadagiti pagnaan.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Inispalnak manipud iti panagririri dagiti tattao. Pinagbalinnak nga ulo kadagiti nasion. Nagserbi kaniak dagiti tattao a saanko nga am-ammo.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
Apaman a mangngegdak, agtulnogda kaniak; napilitan dagiti ganggannaet nga agruknoy kaniak.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Agpigpigerger dagiti ganggannaet a rimmuar kadagiti pagkamkamanganda.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
Sibibiag ni Yahweh; mapadayawan koma ti dakkel a batok. Maitan-ok koma ti Dios ti pannakaisalakanko.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
Daytoy ti Dios nga agibales para kaniak, a mangparparmek kadagiti nasion nga iturturayak.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Nawayawayaannak manipud kadagiti kabusorko! Pudno, intag-aynak iti ngatoen dagiti tattao a bumusor kaniak! Inispalnak kadagiti naranggas a tattao.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Ngarud, agyamanak kenka, Yahweh, kadagiti nasion; agkantaak a mangidaydayaw iti naganmo!
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
It-ited ti Dios ti naindaklan a balligi iti arina, ken ipakpakitana ti kinapudno iti tulagna iti pinulotanna, kenni David ken kadagiti kaputotanna iti agnanayon.