< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
Au maître-chantre. — De David, serviteur de l'Éternel, qui prononça, à la louange de l'Éternel, les paroles de ce cantique, lorsque l'Éternel l'eut délivré de la main de tous ses ennemis et de la main de Saül. Il dit: Je t'aime, ô Éternel, toi qui es ma force!
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
L'Éternel est mon rocher, ma forteresse et mon libérateur! Mon Dieu est le roc où je trouve un refuge, Mon bouclier, mon puissant sauveur, mon rempart!
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Je m'écrie: «Loué soit l'Éternel!» — Et je suis délivré de mes ennemis.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Les liens de la mort m'avaient enveloppé; Les torrents de la destruction m'avaient épouvanté.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Oui, les liens du Sépulcre m'avaient entouré; Les filets de la mort m'avaient surpris. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
Dans ma détresse, j'invoquai l'Éternel, Je criai vers mon Dieu. De son palais, il entendit ma voix; Les cris que je poussais vers lui parvinrent à ses oreilles.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Alors la terre fut ébranlée, et elle trembla; Les fondements des montagnes chancelèrent. Ils s'ébranlèrent, parce que l'Éternel était courroucé.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
La fumée montait de ses narines, Et de sa bouche sortait un feu dévorant: en faisait jaillir des charbons embrasés.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Il inclina les cieux et il descendit, Ayant sous ses pieds une sombre nuée.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Il était monté sur un chérubin, et il volait; Il était porté sur les ailes du vent.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
Il fit des ténèbres sa retraite; déploya autour de lui, comme une tente, Des masses liquides, de sombres nuages.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
Du sein de la splendeur qui le précédait, S'échappaient des nuées, de la grêle et des charbons de feu.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
L'Éternel tonna dans les cieux; Le Très-Haut fit retentir sa voix, Au milieu de la grêle et des charbons de feu.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Il lança ses flèches, et il dispersa mes ennemis; Il lança des éclairs nombreux, et ils furent mis en déroute.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Alors le lit de la mer apparut, Et les fondements du monde furent mis à découvert, A ta voix menaçante, ô Éternel, Au souffle du vent de ta colère.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Dieu étendit sa main d'en haut, et il me saisit; Il me retira des grandes eaux.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
Il me délivra de mon puissant ennemi, De mes adversaires qui étaient plus forts que moi.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Ils m'avaient surpris au jour de ma détresse; Mais l'Éternel a été mon appui.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Il m'a mis au large; Il m'a délivré à cause de son amour pour moi.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
L'Éternel m'a traité selon ma justice; Il a récompensé la pureté de mes mains.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
Car j'ai suivi avec soin les voies de l'Éternel, Et je n'ai pas été infidèle à mon Dieu.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
Tous ses commandements sont présents devant moi, Et je ne m'écarte point de ses préceptes.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
J'ai été sans reproche envers lui, Et je me suis mis en garde contre mon penchant au mal.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Oui, l'Éternel m'a traité selon ma justice, Selon la pureté de mes mains, que ses yeux ont reconnue.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Avec celui qui est, fidèle, tu es fidèle; Avec l'homme intègre, tu es intègre.
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Avec celui qui est pur, tu te montres pur; Mais avec le pervers, tu te joues de sa perversité!
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
Car c'est toi qui sauves le peuple des humbles, Et, qui abaisses les regards des superbes.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
C'est toi qui allumes mon flambeau; C'est l'Éternel, mon Dieu, qui fait resplendir mes ténèbres.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Avec toi j'attaque une troupe armée; Avec mon Dieu je franchis le rempart.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
Les voies du Dieu fort sont parfaites. La parole de l'Éternel est éprouvée: Il est le bouclier de tous ceux qui cherchent leur refuge en lui.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Qui donc est Dieu, sinon l'Éternel? Qui est un rocher, sinon notre Dieu?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
C'est ce Dieu qui me ceint de force, Et qui aplanit mon chemin.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Il rend mes pieds agiles comme ceux des biches, Et il m'affermit sur les sommets.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Il exerce mes mains au combat, Et mes bras bandent un arc, d'airain.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Tu me donnes pour bouclier ton puissant secours. Ta main droite me soutient, Et ta bonté me rend fort.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Tu élargis le chemin sous mes pas, Et mes pieds ne chancellent point.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
Je poursuis mes ennemis, je les atteins, Et je ne reviens qu'après les avoir exterminés.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
Je les écrase, et ils ne peuvent se relever: Ils tombent sous mes pieds.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
Tu m'as ceint de force pour le combat; Tu fais plier sous moi mes adversaires.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Tu fais fuir devant moi mes ennemis; J'extermine ceux qui me haïssent.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
Ils crient, mais personne ne vient les délivrer! Ils crient vers l'Eternel, mais il ne leur répond pas.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Je les broie comme la poussière livrée au vent; Je les balaie comme la boue des rues.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Tu me fais triompher des attaques de mon peuple; Tu me places à la tête des nations. Des peuples inconnus deviennent mes sujets;
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
Dès qu'ils entendent parler de moi, ils se soumettent. Les fils de l'étranger me rendent hommage.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Les fils de l'étranger sont abattus, Et ils sortent tremblants de leurs retraites.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
L'Éternel est vivant! Béni soit mon rocher! Que Dieu, mon libérateur, soit exalté!
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
Ce Dieu m'assure la vengeance; Il m'assujettit les peuples.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Tu me délivres de mes ennemis; Tu m'élèves au-dessus de mes adversaires; Tu me sauves de l'homme violent.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
C'est pourquoi je te louerai, ô Éternel, parmi les nations, Et je psalmodierai à la gloire de ton nom.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
L'Éternel accorde au roi, son élu, de grandes victoires; Il exerce sa miséricorde en faveur de son oint, De David et de sa postérité, à jamais.