< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
Pour le chef musicien. Par David, serviteur de Yahvé, qui adressa à Yahvé les paroles de ce chant, le jour où Yahvé le délivra de la main de tous ses ennemis et de la main de Saül. Il dit, Je t'aime, Yahvé, ma force.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
Yahvé est mon rocher, ma forteresse et mon libérateur; mon Dieu, mon rocher, en qui je trouve refuge; mon bouclier, et la corne de mon salut, ma haute tour.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
J'invoque Yahvé, qui est digne d'être loué; et je suis sauvé de mes ennemis.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Les cordes de la mort m'ont entouré. Les flots de l'impiété m'ont fait peur.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Les cordes du séjour des morts m'entouraient. Les pièges de la mort se sont abattus sur moi. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
Dans ma détresse, j'ai invoqué Yahvé, et j'ai crié à mon Dieu. Il a entendu ma voix hors de sa tempe. Mon cri devant lui est parvenu à ses oreilles.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Alors la terre trembla et s'ébranla. Les fondements des montagnes ont aussi tremblé et ont été ébranlés, parce qu'il était en colère.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
De la fumée sortait de ses narines. Un feu dévorant est sorti de sa bouche. Des charbons ont été allumés par elle.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Il a aussi incliné les cieux, et il est descendu. Une obscurité épaisse était sous ses pieds.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Il était monté sur un chérubin, et il volait. Oui, il a plané sur les ailes du vent.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
Il a fait des ténèbres sa cachette, de son pavillon son entourage, l'obscurité des eaux, les nuages épais des cieux.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
A la clarté qui le précède, les nuages épais ont disparu, des grêlons et des charbons ardents.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Yahvé tonna aussi dans le ciel. Le Très-Haut a fait entendre sa voix: des grêlons et des charbons ardents.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Il envoya ses flèches, et les dispersa. Il les a mis en déroute avec de grands éclairs.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Alors les canaux d'eaux apparurent. Les fondations du monde ont été mises à nu par ta réprimande, Yahvé, au souffle de l'haleine de vos narines.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Il a envoyé d'en haut. Il m'a pris. Il m'a tiré de nombreuses eaux.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
Il m'a délivré de mon ennemi puissant, de ceux qui me haïssaient, car ils étaient trop puissants pour moi.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Ils sont venus sur moi au jour de ma calamité, mais Yahvé était mon soutien.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Il m'a aussi fait sortir dans un grand lieu. Il m'a délivré, car il s'est réjoui de moi.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
L'Éternel m'a récompensé selon ma justice. Selon la pureté de mes mains, il m'a récompensé.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
Car j'ai gardé les voies de l'Éternel, et je ne me suis pas éloigné de mon Dieu par méchanceté.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
Car toutes ses ordonnances étaient devant moi. Je n'ai pas écarté ses statuts de moi.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
J'étais aussi irréprochable avec lui. Je me suis gardé de mon iniquité.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
C'est pourquoi Yahvé m'a récompensé selon ma justice, selon la propreté de mes mains à sa vue.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Avec les miséricordieux, tu te montreras miséricordieux. Avec l'homme parfait, vous vous montrerez parfaite.
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Avec les purs, tu te montreras pur. Avec les tordus, vous vous montrerez astucieux.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
Car tu sauveras le peuple affligé, mais les yeux arrogants, tu les feras tomber.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Car c'est toi qui allumeras ma lampe, Yahvé. Mon Dieu va éclairer mes ténèbres.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Car c'est par toi que j'avance dans une troupe. Par mon Dieu, je saute par-dessus un mur.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
Quant à Dieu, sa voie est parfaite. La parole de Yahvé est éprouvée. Il est un bouclier pour tous ceux qui se réfugient en lui.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Car qui est Dieu, sinon Yahvé? Qui est un rocher, en dehors de notre Dieu,
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
le Dieu qui m'arme de force, et rend mon chemin parfait?
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Il rend mes pieds semblables à des pieds de cerf, et me place sur mes hauts lieux.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Il apprend à mes mains à faire la guerre, pour que mes bras fassent un arc de bronze.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Tu m'as aussi donné le bouclier de ton salut. Ta main droite me soutient. Votre gentillesse m'a rendu grand.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Tu as élargi mes pas sous moi, Mes pieds n'ont pas glissé.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
Je poursuivrai mes ennemis, et je les vaincrai. Je ne me détournerai pas tant qu'ils ne seront pas consommés.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
Je les transpercerai, et ils ne pourront plus se relever. Ils tomberont sous mes pieds.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
Car tu m'as armé de force pour le combat. Tu as soumis à moi ceux qui s'élevaient contre moi.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Tu as aussi fait en sorte que mes ennemis me tournent le dos, afin d'exterminer ceux qui me haïssent.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
Ils ont crié, mais il n'y avait personne pour les sauver; même à Yahvé, mais il ne leur a pas répondu.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Puis je les ai écrasés comme la poussière devant le vent. Je les ai rejetés comme la boue des rues.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Tu m'as délivré de la convoitise du peuple. Tu as fait de moi le chef des nations. Un peuple que je n'ai pas connu me servira.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
Dès qu'ils entendront parler de moi, ils m'obéiront. Les étrangers se soumettront à moi.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Les étrangers disparaîtront, et sortiront en tremblant de leurs forteresses.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
Yahvé est vivant! Béni soit mon rocher. Exalté soit le Dieu de mon salut,
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
même le Dieu qui exécute la vengeance pour moi, et soumet les peuples sous mes ordres.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Il me sauve de mes ennemis. Oui, tu m'élèves au-dessus de ceux qui s'élèvent contre moi. Tu me délivres de l'homme violent.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
C'est pourquoi je te louerai, Yahvé, parmi les nations, et chanteront les louanges de ton nom.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
Il accorde une grande délivrance à son roi, et fait preuve de bonté envers ses oints, à David et à sa descendance, pour toujours.