< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
To the chief Musician, A Psalm of David, the servant of the LORD, who spoke to the LORD the words of this song in the day that the LORD delivered him from the hand of all his enemies, and from the hand of Saul: And he said, I will love thee, O LORD, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
The LORD is my rock, and my fortress, and my deliverer; my God, my strength, in whom I will trust; my buckler, and the horn of my salvation, and my high tower.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon the LORD, who is worthy to be praised: so shall I be saved from my enemies.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The sorrows of death surrounded me, and the floods of ungodly men made me afraid.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
The sorrows of hell surrounded me: the snares of death seized me. (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
In my distress I called upon the LORD, and cried to my God: he heard my voice out of his temple, and my cry came before him, even into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then the earth shook and trembled; the foundations also of the hills moved and were shaken, because he was angry.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke out of his nostrils, and fire out of his mouth devoured: coals were kindled by it.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
He bowed the heavens also, and came down: and darkness was under his feet.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon a cherub, and flew: yea, he flew upon the wings of the wind.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
He made darkness his secret place; his pavilion around him was dark waters and thick clouds of the skies.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
At the brightness that was before him his thick clouds passed, hail stones and coals of fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
The LORD also thundered in the heavens, and the Highest gave his voice; hail stones and coals of fire.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Yea, he sent out his arrows, and scattered them; and he shot out lightnings, and destroyed them.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Then the channels of waters were seen, and the foundations of the world were uncovered at thy rebuke, O LORD, at the blast of the breath of thy nostrils.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from above, he took me, he drew me out of many waters.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my strong enemy, and from them who hated me: for they were too strong for me.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They came upon me in the day of my calamity: but the LORD was my stay.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
He brought me forth also in a large place; he delivered me, because he delighted in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
The LORD rewarded me according to my righteousness; according to the cleanness of my hands hath he recompensed me.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the ways of the LORD, and have not wickedly departed from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his judgments were before me, and I did not put away his statutes from me.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
I was also upright before him, and I kept myself from my iniquity.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Therefore hath the LORD recompensed me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in his sight.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the merciful thou wilt show thyself merciful; with an upright man thou wilt show thyself upright;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
With the pure thou wilt show thyself pure; and with the perverse thou wilt contend.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For thou wilt save the afflicted people; but wilt bring down high looks.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For thou wilt light my lamp: the LORD my God will enlighten my darkness.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by thee I have run through a troop; and by my God have I leaped over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
As for God, his way is perfect: the word of the LORD is tried: he is a buckler to all those that trust in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God except the LORD? or who is a rock except our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
It is God that girdeth me with strength, and maketh my way perfect.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He maketh my feet like hinds’ feet, and setteth me upon my high places.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He teacheth my hands to war, so that a bow of steel is broken by my arms.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Thou hast also given me the shield of thy salvation: and thy right hand hath held me up, and thy gentleness hath made me great.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Thou hast enlarged my steps under me, that my feet did not slip.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I have pursued my enemies, and overtaken them: neither did I turn again till they were consumed.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I have wounded them that they were not able to rise: they have fallen under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
For thou hast girded me with strength to battle: thou hast subdued under me those that rose up against me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Thou hast also given me the necks of my enemies; that I might destroy them that hate me.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They cried, but there was none to save them: even to the LORD, but he answered them not.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Then I beat them small as the dust before the wind: I cast them out as the dirt in the streets.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Thou hast delivered me from the strivings of the people; and thou hast made me the head of the heathen: a people whom I have not known shall serve me.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
As soon as they hear of me, they shall obey me: the strangers shall submit themselves to me.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The strangers shall fade away, and come trembling out of their fortresses.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
The LORD liveth; and blessed be my rock; and let the God of my salvation be exalted.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
It is God that avengeth me, and subdueth the people under me.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
He delivereth me from my enemies: yea, thou liftest me up above those that rise up against me: thou hast delivered me from the violent man.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore will I give thanks to thee, O LORD, among the heathen, and sing praises to thy name.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
He giveth great deliverance to his king; and showeth mercy to his anointed, to David, and to his seed for evermore.

< Masalimo 18 >