< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
For the Chief Musician. [A Psalm] of David the servant of the LORD, who spake unto the LORD the words of this song in the day that the LORD delivered him from the hand of all his enemies, and from the hand of Saul: and he said, I love thee, O LORD, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
The LORD is my rock, and my fortress, and my deliverer; my God, my strong rock, in him will I trust; my shield, and the horn of my salvation, my high tower.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon the LORD, who is worthy to be praised: so shall I be saved from mine enemies.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The cords of death compassed me, and the floods of ungodliness made me afraid.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
The cords of Sheol were round about me: the snares of death came on me. (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
In my distress I called upon the LORD, and cried unto my God: he heard my voice out of his temple, and my cry before him came into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then the earth shook and trembled, me foundations also of the mountains moved and were shaken, because he was wroth.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke out of his nostrils, and fire out of his mouth devoured: coals were kindled by it.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
He bowed the heavens also, and came down, and thick darkness was under his feet.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon a cherub, and did fly, yea, he flew swiftly upon the wings of the wind.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
He made darkness his hiding place, his pavilion round about him; darkness of waters, thick clouds of the skies.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
At the brightness before him his thick clouds passed, hailstones and coals of fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
The LORD also thundered in the heavens, and the Most High uttered his voice; hailstones and coals of fire.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent out his arrows, and scattered them; yea, lightnings manifold, and discomfited them.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Then the channels of waters appeared, and the foundations of the world were laid bare, at thy rebuke, O LORD, at the blast of the breath of thy nostrils.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from on high, he took me; he drew me out of many waters.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my strong enemy, and from them that hated me, for they were too mighty for me.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They came upon me in the day of my calamity: but the LORD was my stay.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
He brought me forth also into a large place; he delivered me, because he delighted in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
The LORD rewarded me according to my righteousness; according to the cleanness of my hands hath he recompensed me.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the ways of the LORD, and have not wickedly departed from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his judgments were before me, and I put not away his statutes from me.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
I was also perfect with him, and I kept myself from mine iniquity.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Therefore hath the LORD recompensed me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in his eyesight.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the merciful thou wilt shew thyself merciful; with the perfect man thou wilt shew thyself perfect;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
With the pure thou wilt shew thyself pure; and with the perverse thou wilt shew thyself froward.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For thou wilt save the afflicted people; but the haughty eyes thou wilt bring down.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For thou wilt light my lamp: the LORD my God will lighten my darkness.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by thee I run upon a troop; and by my God do I leap over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
As for God, his way is perfect: the word of the LORD is tried; he is a shield unto all them that trust in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God, save the LORD? and who is a rock, beside our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
The God that girdeth me with strength, and maketh my way perfect.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He maketh my feet like hinds’ [feet]: and setteth me upon my high places,
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He teacheth my hands to war; so that mine arms do bend a bow of brass.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
Thou hast also given me the shield of thy salvation: and thy right hand hath holden me up, and thy gentleness hath made me great.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Thou hast enlarged my steps under me, and my feet have not slipped.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I will pursue mine enemies, and overtake them: neither will I turn again till they are consumed.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I will smite them through that they shall not be able to rise: they shall fall under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
For thou hast girded me with strength unto the battle: thou hast subdued under me those that rose up against me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
Thou hast also made mine enemies turn their backs unto me, that I might cut off them that hate me.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They cried, but there was none to save: even unto the LORD, but he answered them not.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Then did I beat them small as the dust before the wind: I did cast them out as the mire of the streets.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Thou hast delivered me from the strivings of the people; thou hast made me the head of the nations: a people whom I have not known shall serve me.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
As soon as they hear of me they shall obey me: the strangers shall submit themselves unto me.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The strangers shall fade away, and shall come trembling out of their close places.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
The LORD liveth; and blessed be my rock; and exalted be the God of my salvation:
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
Even the God that executeth vengeance for me, and subdueth peoples under me.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
He rescueth me from mine enemies: yea, thou liftest me up above them that rise up against me: thou deliverest me from the violent man.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore I will give thanks unto thee, O LORD, among the nations, and will sing praises unto thy name.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
Great deliverance giveth he to his king; and sheweth lovingkindness to his anointed, to David and to his seed, for evermore.

< Masalimo 18 >