< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
“To the chief musician, by the servant of the Lord, by David, who spoke unto the Lord the words of this song on the day that the Lord had delivered him out of the power of all his enemies, and from the hand of Saul; And he said,” I ever love thee, O Lord, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
The Lord is my rock, and my fortress, and my deliverer; my God, my rock, in whom I trust; my shield, and the horn of my salvation, and my high tower.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Praised, I cried, be the Lord, and from my enemies was I saved.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The bonds of death encompassed me, and the floods of destruction made me afraid.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
The bonds of hell encircled me: the snares of death seized on me. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
[When] in my distress I called upon the Lord, and unto my God I cried: he heard from his temple my voice, and my complaint came before him, even into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then shook and trembled the earth; and the foundations of the mountains were moved; and they were shaken, because he was wroth.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Smoke went up in his anger and consuming fire out of his mouth: coals flamed forth from him.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
And he bent the heavens, and came down: and thick darkness was under his feet:
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon a cherub, and flew along, and he flitted by upon the wings of the wind.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
He made darkness his hiding-place, round about him as his pavilion, dark waters, thick clouds of the skies.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
From the brightness before him his thick clouds passed away, [with] hail-stones and coals of fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
And the Lord thundered in the heavens, and the Most High uttered forth his voice, [with] hail-stones and coals of fire.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent out his arrows, and scattered them; and he shot forth lightnings, and discomfited them.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
And then were seen the channels of the waters, and there were laid open the foundations of the world, through thy rebuke, O Lord, through the blast of the breath of thy nostrils.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He stretched out from above [his hand], he took me; he drew me out from mighty waters.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my enemy, the strong, and from those that hated me, when they were too mighty for me.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They overcame me on the day of my calamity; but the Lord became my stay.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
And he brought me forth into a large space; he delivered me, because he had delight in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
The Lord rewarded me according to my righteousness; according to the purity of my hands did he recompense me.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the ways of the Lord, and have not wickedly departed from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his ordinances were before me, and his statutes had I not put away from me.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
I was also upright with him, and I guarded myself against my iniquity.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Therefore did the Lord recompense me according to my righteousness, according to the purity of my hands before his eyes.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the kind thou wilt show thyself kind; with the upright man thou wilt show thyself upright;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
With the pure thou wilt show thyself pure; and with the perverse thou wilt wage a contest.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For thou wilt indeed save the afflicted people; but haughty eyes wilt thou bring down.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For thou wilt cause my light to shine: the Lord my God will enlighten my darkness.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For [aided] by thee I run through a troop; and [helped] by my God I leap over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
As for God, —his way is perfect; the word of the Lord is tried: he is a shield to all those that trust in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God save the Lord? or who is a rock beside our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
He is the God that girdeth me with strength, and rendereth my way unobstructed.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He maketh my feet like those of the hinds, and upon my high-places he causeth me to stand.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He teacheth my hands for the war, so that a brazen bow is bent by my arms.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
And thou gavest me the shield of thy salvation, and thy right hand supported me: and thy meekness hath made me great.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Thou enlargest my steps under me, so that my joints do not slip.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I pursue my enemies, and overtake them; and I return not again till I have made an end of them.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I crush them that they are not able to rise: they fall under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
For thou hast girded me with strength for the war: thou subduest my opponents under me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
And my enemies thou causest to turn their back to me; and those that hate me, —that I may destroy them.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They cry, but there is none to help; unto the Lord, —but he answereth them not.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
And I beat them small as the dust before the wind: like the dirt in the streets do I cast them out.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Thou deliverest me from the contests of the people; thou appointest me to be the head of nations: a people that I know not shall serve me.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
As soon as their ear heareth they shall be obedient to me: the children of the stranger shall utter flattery unto me.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The children of the stranger shall fade away, and come forth trembling out of their close places.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
The Lord liveth, and blessed be my Rock; and exalted be the God of my salvation;
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
The God that granteth me vengeance, and subdueth nations under me;
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
That delivereth me from my enemies: also above my opponents thou liftest me up; thou deliverest me from the man of violence.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore will I give thanks unto thee among the nations, O Lord, and unto thy name will I sing praises, —
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
[To him] that maketh great the salvation of his king, and who sheweth kindness to his anointed, to David, and to his seed for ever.