< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
To the chief Musician. [A Psalm] of David, the servant of Jehovah, who spoke to Jehovah the words of this song in the day that Jehovah had delivered him out of the hand of all his enemies and out of the hand of Saul. And he said, I will love thee, O Jehovah, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
Jehovah is my rock, and my fortress, and my deliverer; my God, my rock, in whom I will trust; my shield, and the horn of my salvation, my high tower.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon Jehovah, who is to be praised: so shall I be saved from mine enemies.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The bands of death encompassed me, and torrents of Belial made me afraid.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
The bands of Sheol surrounded me, the cords of death encountered me. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
In my distress I called upon Jehovah, and I cried out to my God; he heard my voice out of his temple, and my cry came before him, into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then the earth shook and quaked, and the foundations of the mountains trembled and shook, because he was wroth.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke out of his nostrils, and fire out of his mouth devoured: coals burned forth from it.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
And he bowed the heavens, and came down; and darkness was under his feet.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon a cherub and did fly; yea, he flew fast upon the wings of the wind.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
He made darkness his secret place, his tent round about him: darkness of waters, thick clouds of the skies.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
From the brightness before him his thick clouds passed forth: hail and coals of fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
And Jehovah thundered in the heavens, and the Most High uttered his voice: hail and coals of fire.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent his arrows, and scattered [mine enemies]; and he shot forth lightnings, and discomfited them.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
And the beds of the waters were seen, and the foundations of the world were uncovered at thy rebuke, Jehovah, at the blast of the breath of thy nostrils.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He reached forth from above, he took me, he drew me out of great waters:
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my strong enemy, and from them that hated me; for they were mightier than I.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They encountered me in the day of my calamity, but Jehovah was my stay.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
And he brought me forth into a large place; he delivered me, because he delighted in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Jehovah hath rewarded me according to my righteousness; according to the cleanness of my hands hath he recompensed me.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the ways of Jehovah, and have not wickedly departed from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his ordinances were before me, and I did not put away his statutes from me;
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
And I was upright with him, and kept myself from mine iniquity.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
And Jehovah hath recompensed me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in his sight.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the gracious thou dost shew thyself gracious; with the upright man thou dost shew thyself upright;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
With the pure thou dost shew thyself pure; and with the perverse thou dost shew thyself contrary.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For it is thou that savest the afflicted people; but the haughty eyes wilt thou bring down.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For it is thou that makest my lamp to shine: Jehovah my God enlighteneth my darkness.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by thee I have run through a troop; and by my God have I leaped over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
As for God, his way is perfect; the word of Jehovah is tried: he is a shield to all that trust in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God save Jehovah? and who is a rock if not our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
The God who girdeth me with strength, and maketh my way perfect,
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Who maketh my feet like hinds' [feet], and setteth me upon my high places;
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Who teacheth my hands to war, and mine arms bend a bow of brass;
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
And thou didst give me the shield of thy salvation, and thy right hand held me up; and thy condescending gentleness hath made me great.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
Thou didst enlarge my steps under me, and mine ankles have not wavered.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I pursued mine enemies, and overtook them; and I turned not again till they were consumed.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I crushed them, and they were not able to rise: they fell under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
And thou girdedst me with strength to battle; thou didst subdue under me those that rose up against me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
And mine enemies didst thou make to turn their backs unto me, and those that hated me I destroyed.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They cried, and there was none to save; — unto Jehovah, and he answered them not.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
And I did beat them small as dust before the wind; I did cast them out as the mire of the streets.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Thou hast delivered me from the strivings of the people; thou hast made me the head of the nations: a people I knew not doth serve me.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
At the hearing of the ear, they obey me: strangers come cringing unto me.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Strangers have faded away, and they come trembling forth from their close places.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
Jehovah liveth; and blessed be my rock; and exalted be the God of my salvation,
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
The God who hath avenged me, and hath subjected the peoples to me;
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Who hath delivered me from mine enemies: yea, thou hast lifted me up above them that rose up against me; from the man of violence hast thou delivered me.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore will I give thanks to thee, Jehovah, among the nations, and will sing psalms to thy name.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
[It is he] who giveth great deliverances to his king, and sheweth loving-kindness to his anointed, to David, and to his seed for evermore.