< Masalimo 18 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
To the chief music-maker. Of the servant of the Lord, of David, who said the words of this song to the Lord on the day when the Lord made him free from the hand of all his haters, and from the hand of Saul; and he said, I will give you my love, O Lord, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
The Lord is my Rock, my walled town, and my saviour; my God, my Rock, in him will I put my faith; my breastplate, and the horn of my salvation, and my high tower.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will send up my cry to the Lord, who is to be praised; so will I be made safe from those who are against me.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The cords of death were round me, and the seas of evil put me in fear.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
The cords of hell were round me: the nets of death came on me. (Sheol )
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
In my trouble my voice went up to the Lord, and my cry to my God: my voice came to his hearing in his holy Temple, and my prayer came before him, even into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then trouble and shock came on the earth; and the bases of the mountains were moved and shaking, because he was angry.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke from his nose, and a fire of destruction from his mouth: flames were lighted by it.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
The heavens were bent, so that he might come down; and it was dark under his feet.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he went in flight through the air, seated on a storm-cloud: going quickly on the wings of the wind.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
He made the dark his secret place; his tent round him was the dark waters and thick clouds of the skies.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
Before his shining light his dark clouds went past, raining ice and fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
The Lord made thunder in the heavens, and the voice of the Highest was sounding out: a rain of ice and fire.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
He sent out his arrows, driving them in all directions; by his flames of fire they were troubled.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
Then the deep beds of the waters were seen, and the bases of the world were uncovered, because of your words of wrath, O Lord, because of the breath from your mouth.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from on high, he took me, pulling me out of great waters.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He made me free from my strong hater, and from those who were against me, because they were stronger than I.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They came on me in the day of my trouble; but the Lord was my support.
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
He took me out into a wide place; he was my saviour because he had delight in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
The Lord gives me the reward of my righteousness, because my hands are clean before him.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the ways of the Lord; I have not been turned away in sin from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his decisions were before me, and I did not put away his laws from me.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
And I was upright before him, and I kept myself from sin.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
Because of this the Lord has given me the reward of my righteousness, because my hands are clean in his eyes.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
On him who has mercy you will have mercy; to the upright you will be upright;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
He who is holy will see that you are holy; but to the man whose way is not straight you will be a hard judge.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For you are the saviour of those who are in trouble; but eyes full of pride will be made low.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
You, O Lord, will be my light; by you, my God, the dark will be made bright for me.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
By your help I have made a way through the wall which was shutting me in; by the help of my God I have gone over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
As for God, his way is completely good; the word of the Lord is tested; he is a breastplate for all those who put their faith in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God but the Lord? or who is a Rock but our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
God puts a strong band about me, guiding me in a straight way.
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He makes my feet like roes' feet, and puts me on high places.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He makes my hands expert in war, so that a bow of brass is bent by my arms.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
You have given me the breastplate of your salvation: your right hand has been my support, and your mercy has made me great.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
You have made my steps wide under me, so that my feet are kept from slipping.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I go after my haters and overtake them; not turning back till they are all overcome.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I will give them wounds, so that they are not able to get up: they are stretched under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
For I have been armed by you with strength for the fight: you have made low under me those who come out against me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
By you their backs are turned in flight, so that my haters are cut off.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They were crying out, but there was no one to come to their help: even to the Lord, but he gave them no answer.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Then they were crushed as small as dust before the wind; they were drained out like the waste of the streets.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
You have made me free from the fightings of the people; you have made me the head of the nations: a people of whom I had no knowledge will be my servants.
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
From the time when my name comes to their ears they will be ruled by me: men of other countries will, with false hearts, put themselves under my authority.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
They will be wasting away, they will come out of their secret places shaking with fear.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
The Lord is living; praise be to my Rock, and let the God of my salvation be honoured.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
It is God who sends punishment on my haters, and puts peoples under my rule.
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
He makes me free from my haters; I am lifted up over those who come up against me: you have made me free from the violent man.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Because of this I will give you praise, O Lord, among the nations, and will make a song of praise to your name.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
Great salvation does he give to his king; he has mercy on the king of his selection, David, and on his seed for ever.