< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Molitev Davidova: Čuj, Gospod, pravico, poslušaj vpitje moje; uho nagni molitvi moji brez ustnic zvijačnih.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Od obličja tvojega izidi pravica moja; oči tvoje naj gledajo, kar je pravično.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Ko bodeš preiskal srce moje, obiskal ponoči, preskušal me, ne najdeš; kar mislim, ne prestopi mojih ust.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Pri delih človeških, po besedi ustnic tvojih opazujem steze silovitega.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Ohrani korake moje na stezah svojih, da ne zaidejo moje noge.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Jaz te kličem, ker me slišiš, Bog mogočni; nagni k meni uho svoje, poslušaj govor moj.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Odloči milosti svoje, o ti, ki otimaš preganjalcev pribegajoče na desnico tvojo.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Hrani me kakor zenico v očesu; sè senco peroti svojih skrivaj me:
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
Zaradi krivičnih, ki me napadajo, sovražnikov mojih glavnih, ki me obdajajo.
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
Mast svojo masté, z usti svojimi govoré prevzetno:
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
Hojo našo zdaj obdajajo nam; oči svoje obračajo vpirajoč v tla.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Podoba je vsakega kakor leva želečega zgrabiti, in kakor mladega leva čepečega v zakotji.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Vstani, Gospod, prehítí obličje njegovo; trešči ga, izpuli dušo mojo z mečem svojim krivičnemu.
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
Ljudém izpuli v roko svojo, Gospod, ljudém od svetá, katerih delež je v tem življenji, katerim trebuh polniš sè skrivnim zakladom svojim; sitijo se sinovi in preobilost svojo zapuščajo otrokom svojim.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Jaz bodem v pravičnosti videl obličje tvoje, sitil se bodem, ko se zbudim, s podobo tvojo.

< Masalimo 17 >