< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Umkhuleko kaDavida. Zwana, Oh Thixo, ukuncenga kwami okulungileyo; lalela ukukhala kwami. Zwana umkhuleko wami, kawusuki ezindebeni ezikhohlisayo.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Ukugezwa kwami ecaleni kakuvele kuwe; sengathi amehlo Akho angabona lokho okuqondileyo.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Udungulule inhliziyo yami wangihlola ebusuku wangilinga, kawuyikufumana lutho olubi engiluhlelileyo; sengizimisele ukuthi umlomo wami ungenzi sono.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Mayelana lezenzo zabantu, mina ngizazithiba ezindleleni zobudlwangudlwangu ngelizwi lezindebe zakho.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Izinyathelo zami zalela ezindleleni zakho; inyawo zami kazizange zitshelele.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Ngikhala kuwe, Oh Nkulunkulu ngoba uzangiphendula; ngilalela uzwe umkhuleko wami.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Tshengisa ukumangalisa kothando lwakho olukhulu, wena osindisa ngesandla sakho sokunene, labo ababalekela kuwe ezitheni zabo.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Ngilondoloza njengegugu lakho; ngifihla emthunzini wamaphiko akho
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
kwababi abangihlaselayo, ezitheni zami ezimbi ezingihanqileyo.
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
Bagcika inhliziyo zabo ezingelazwelo, lemilomo yabo ikhuluma iqholoza.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
Sebeze bangithola, manje sebengihanqile bangiqhuzulele amehlo bafuna ukungilahla phansi.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Banjengesilwane silambele loba yini esingayidumela, njengesilwane esesabekayo siquthile sicatshile.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Phakama, Oh Thixo, basukele, balahle phansi; ngilamulela kwababi ngenkemba yakho.
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
Oh Thixo, ngisindisa ngesandla sakho ebantwini abanjalo, ebantwini bakulumhlaba omvuzo wabo ukuyonale impilo. Udedisa iphango lalabo obathandayo; amadodana abo akhomba ngophakathi; baqoqela abantwababo inotho.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Mina-ke ngenxa yokulunga ngizabubona ubuso bakho; ngizakuthi ekuvukeni kwami nganeliswe yikubona isimo sakho.

< Masalimo 17 >